< Salamans Mācītājs 1 >
1 Dāvida dēla, Jeruzālemes ķēniņa, mācības vārdi.
Mawu a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya ku Yerusalemu:
2 Niecība vien, saka tas mācītājs, niecība vien, viss ir niecība.
“Zopandapake! Zopandapake!” atero Mlaliki. “Zopandapake kotheratu! Zopandapake.”
3 Kāds labums cilvēkam atlec no visa viņa grūta darba, ar ko viņš nodarbojās pasaulē.
Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zake zonse zimene amasautsidwa nazo pansi pano?
4 Cits dzimums aiziet un cits dzimums nāk; bet zeme pastāv mūžīgi.
Mibado imabwera ndipo mibado imapita, koma dziko lapansi limakhalapobe nthawi zonse.
5 Saule lec un saule noiet un steidzās uz savu vietu, kur tā atkal uzlec.
Dzuwa limatuluka ndipo dzuwa limalowa ndipo limapita mwamsanga kumene limatulukira.
6 Vējš iet pret dienasvidu un iet apkārt pret ziemeļa pusi; tas pūš visapkārt griezdamies un riņķī apgriežas atpakaļ.
Mphepo imawombera cha kummwera ndi kukhotera cha kumpoto; imawomba mozungulirazungulira, kumangobwererabwerera komwe yachokera.
7 Visas upes ietek jūrā, tomēr jūra netop pilnāka. Tai vietā, no kurienes upes nāk, turp tās atkal atgriežas atpakaļ.
Mitsinje yonse imakathira ku nyanja, koma nyanjayo sidzaza; kumene madziwo amachokera, amabwereranso komweko.
8 Visās lietās ir tik daudz grūtuma, ka neviens to nevar izteikt. Acīm nepietiek redzot, un ausīm nepietiek dzirdot.
Zinthu zonse ndi zotopetsa, kutopetsa kwake ndi kosaneneka. Maso satopa ndi kuona kapena khutu kukwaniritsidwa ndi kumva.
9 Kas jau ir bijis, tas vēl būs; un kas jau ir darīts, tas vēl taps darīts; un it nekā jauna nav pasaulē.
Zomwe zinalipo kale zidzakhalaponso, zomwe zinachitika kale zidzachitikanso. Ndiye kuti chatsopano palibiretu pansi pano.
10 Vai ir kas, par ko varētu sacīt: redzi, tas ir jauns? Tas jau ilgi bijis vecos laikos, kas bijuši priekš mums.
Kodi chilipo chinthu chimene wina anganene kuti, “Taona! Ichi ndiye chatsopano?” Chinalipo kale, kalekale; chinalipo ife kulibe.
11 Kas pagājis, netop pieminēts; un kas nāks, to arī nepieminēs tie, kas pēc tam būs.
Anthu akale sakumbukiridwa, ngakhale amene adzabwera mʼtsogolomu sadzakumbukiridwa ndi iwo amene adzabwere pambuyo pawo.
12 Es, tas mācītājs, biju ķēniņš pār Israēli Jeruzālemē.
Ine, Mlalikine, ndinali mfumu ya Israeli mu Yerusalemu.
13 Un apņēmos savā sirdī, ar gudrību izmeklēt un izdibināt visu, kas apakš debess notiek. Šo grūto pūliņu Dievs cilvēku bērniem ir uzlicis, lai ar to nopūlējās.
Ndinayika mtima wanga pophunzira ndi kufunafuna mwa nzeru zinthu zonse zimene zimachitika pansi pa thambo. Ndi ntchito yolemetsa ndithu imene Mulungu anayipereka kwa anthu!
14 Es uzlūkoju visus darbus, kas pasaulē notiek, un redzi, viss bija niecība un grābstīšanās pēc vēja.
Ine ndaona zinthu zonse zochitika pansi pano; zinthu zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
15 Kas līks, nevar palikt taisns; un kā nav, to nevar skaitīt.
Chinthu chokhota sichingathe kuwongoledwa; chimene palibe sichingathe kuwerengedwa.
16 Es runāju savā sirdī un sacīju: redzi, es gudrībā esmu augsti cēlies un pieņēmies vairāk nekā visi, kas priekš manis bijuši Jeruzālemē, un mana sirds ir redzējusi gudrības un zinības papilnam.
Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Taona, ine ndakula ndi kukhala wa nzeru zochuluka kupambana aliyense amene analamulirapo Yerusalemu ndisanabadwe; ndaphunzira nzeru zochuluka ndi luntha.”
17 Un es apņēmos savā sirdī, atzīt gudrību un zinību, neprātību un ģeķību. Bet es samanīju, ka tā ir grābstīšanās pēc vēja.
Ndipo ndinadzipereka kuti ndithe kumvetsa kuti nzeru nʼchiyani, misala nʼchiyani, uchitsiru nʼchiyani, koma ndinazindikira ichi, kuti kuteronso nʼkungodzivuta chabe.
18 Jo kur daudz gudrības, tur ir daudz grūtības, un jo vairāk atzīšanas, jo vairāk bēdu.
Pakuti nzeru zochuluka zimabweretsa chisoni chochulukanso: chidziwitso chochuluka, zowawa zochulukanso.