< Amosa 4 >
1 Klausiet šo vārdu, Basanas govis, kas Samarijas kalnā, kas nospaida mazos, satriec nabagus, kas uz saviem kungiem saka: nesiet šurp, ka dzeram.
Imvani mawu awa, inu ngʼombe zazikazi za ku Basani, okhala pa Phiri la Samariya, inu akazi amene mumapondereza anthu osauka ndi kuzunza anthu osowa ndi kumanena kwa amuna anu kuti, “Tipatseni zakumwa!”
2 Tas Kungs Dievs ir zvērējis pie Sava svētuma: redzi, dienas nāks pār jums, ka jūs aizvilks ar kāšiem un jūsu beidzamos ar zivju makšķerēm,
Ambuye Yehova, mwa kuyera mtima kwake walumbira kuti, “Nthawi idzafika ndithu pamene adzakukokani ndi ngowe, womaliza wa inu adzakokedwa ndi mbedza.
3 Un jūs iziesiet caur mūru plaisām, ikviena taisni projām, un tapsiet nomestas pret Armonu, saka Tas Kungs.
Mudzatulukira mʼmingʼalu ya pa khoma aliyense payekhapayekha, ndipo mudzatayidwa ku Harimoni,” akutero Yehova.
4 Ejat uz Bēteli un grēkojiet! (Ejat) uz Gilgalu un vairojiet pārkāpšanu! Un nesiet savus upurus rītos, savas desmitās(tiesas) ik trešo dienu,
“Bwerani ku Beteli mudzachimwe; ndi ku Giligala kuti mudzapitirize kuchimwa. Bweretsani nsembe zanu mmawa uliwonse, bweretsani chakhumi chanu masiku atatu aliwonse.
5 Un kvēpinājiet pateicības upurus no raudzēta, un izsauciet labprātības upurus, liekat to dzirdēt! Jo tā tas jums patīk, Israēla bērni, saka Tas Kungs Dievs.
Wotchani buledi wokhala ndi yisiti ngati nsembe yachiyamiko ndi kumanyadira poyera za zopereka zanu zaufulu. Inu Aisraeli, zinyadireni nsembezo, pakuti izi ndi zimene mumakonda kuchita,” akutero Ambuye Yehova.
6 Tāpēc es arīdzan jūsu zobiem esmu devis mieru visās jūsu pilsētās un maizes trūkumu visās jūsu vietās; tomēr jūs pie Manis neesat atgriezušies, saka Tas Kungs.
“Ndine amene ndinakusendetsani milomo mʼmizinda yanu yonse, ndipo munasowa chakudya mʼmizinda yanu. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
7 Un arī lietu Es jums esmu aizturējis, kad vēl trīs mēneši bija līdz pļaujamam laikam, un esmu licis līt pār vienu pilsētu, bet pār otru ne, viens zemes gabals aplija, bet otrs gabals sakalta, kur lietus nelija.
“Ndinenso amene ndinamanga mvula patangotsala miyezi itatu kuti mukolole. Ndinagwetsa mvula pa mzinda wina, koma pa mzinda wina ayi, mvula inkagwa pa munda wina; koma sinagwe pa munda wina ndipo mbewu zinawuma.
8 Un divas, trīs pilsētas vilkās uz vienu pilsētu, ūdeni dzert, bet nedabūja nodzerties; taču jūs pie Manis neesat atgriezušies, saka Tas Kungs.
Anthu ankayenda mzinda ndi mzinda kufuna madzi, koma sanapeze madzi okwanira kumwa. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
9 Es jūs esmu sitis ar bulu un ar rūsu, un siseņi ēda visu, kas aug jūsu dārzos un jūsu vīna dārzos un uz jūsu vīģes kokiem un eļļas kokiem, taču jūs pie Manis neesat atgriezušies, saka Tas Kungs.
“Nthawi zambiri ndinakantha mbewu zanu ndiponso minda ya mpesa, ndinayikantha ndi chinsikwi ndiponso ndi chiwawu. Dzombe linawononga mikuyu yanu ndi mitengo ya olivi. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
10 Es esmu sūtījis mēri jūsu vidū, kā Ēģiptes zemē, Es nokāvu jūsu jaunekļus caur zobenu un liku jūsu zirgus aizvest, un jūsu karaspēka smaržai Es liku uzkāpt jūsu nāsīs; taču jūs pie Manis neesat atgriezušies, saka Tas Kungs.
“Ine ndinabweretsa miliri pakati panu monga ndinachitira ku Igupto. Ndinapha anyamata anu ndi lupanga, ndinapereka akavalo anu kwa adani. Ndinakununkhitsani fungo la mitembo lochokera mʼmisasa yanu ya nkhondo. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
11 Es esmu sūtījis postu jūsu vidū, kā Dievs postījis Sodomu un Gomoru un jūs bijāt kā pagale izrauta no uguns, taču jūs neesat atgriezušies pie Manis, saka Tas Kungs.
“Ndinawononga ena mwa inu monga ndinawonongera Sodomu ndi Gomora. Inu munali ngati chikuni choyaka chimene chafumulidwa pa moto. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
12 Tādēļ Es tev tā darīšu, Israēl! Kad Es tev tā gribu darīt, nu tad sataisies, Israēl, savam Dievam pretim!
“Choncho izi ndi zimene ndidzakuchitire iwe Israeli, chifukwa ndidzakuchitira zimenezi, konzekera kukumana ndi Mulungu wako, iwe Israeli.”
13 Jo redzi, kas taisa kalnus, rada vēju un cilvēkam dara zināmu, kas viņa domās, kas par rīta gaismu dara tumsu un staigā pār zemes augstumiem, Kungs Dievs Cebaot ir Viņa vārds.
Iye amene amawumba mapiri, amalenga mphepo, ndipo amawululira munthu za mʼmaganizo ake, Iye amene amasandutsa usana kuti ukhale mdima, ndipo amayenda pa zitunda za dziko lapansi, dzina lake ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.