< Pēteŗa 1. Vēstule 2 >

1 Bet nu atstājiet visu ļaunumu un visu viltību un liekulību un skaudību un visas aprunāšanas;
Choncho, lekani zoyipa zonse, chinyengo chilichonse, chiphamaso, nsanje ndi kusinjirira kulikonse.
2 Tā kā jaunpiedzimuši bērniņi iekārojaties to garīgo bezviltīgo pienu, ka jūs caur to uzaugat,
Monga makanda obadwa kumene amalirira mkaka, inunso muzilakalaka mkaka weniweni wauzimu, kuti mukule ndi kukufikitsani ku chipulumutso chanu,
3 Ja jūs esat baudījuši, ka Tas Kungs ir laipnīgs;
pakuti tsopano mwalawadi kuti Ambuye ndi wabwino.
4 Pie Tā jūs esat nākuši kā pie dzīva akmens, gan atmests no cilvēkiem, bet izredzēts un dārgs pie Dieva.
Pamene mukubwera kwa Iye, amene ndi Mwala wa moyo, umene anthu anawukana, koma Mulungu anawusankha kuti ndi wa mtengowapatali,
5 Un jūs paši arīdzan kā dzīvi akmeņi topat uztaisīti par garīgu namu un svētu priesterību, garīgus upurus upurēt, kas Dievam ir pieņēmīgi caur Jēzu Kristu.
inunso, mukhale ngati miyala ya moyo yoti Mulungu amangire nyumba yake yauzimu kuti mukhale ansembe opatulika, opereka nsembe zauzimu zovomerezeka ndi Mulungu mwa Yesu Khristu.
6 Jo rakstos stāv(rakstīts): redzi, Es lieku Ciānā izredzētu, it dārgu stūra akmeni; un kas tic uz Viņu, tas nepaliks kaunā.
Pakuti mʼMalemba mwalembedwa kuti, “Taonani, ndikuyika mwala wa maziko mu Ziyoni, wosankhika ndi wamtengowapatali. Amene akhulupirira Iye sadzachititsidwa manyazi.”
7 Tad nu jums, kas ticat, Viņš ir dārgs; bet tiem neklausīgiem tas akmens, ko tie nama taisītāji atmetuši, kas ir palicis par stūra akmeni, ir arī klupšanas akmens un piedauzīšanās klints,
Tsono kwa inu okhulupirira, mwalawo ndi wamtengowapatali. Koma kwa amene sakhulupirira, “Mwala umene amisiri anawukana wasanduka mwala wa maziko,
8 Tiem, kas neklausīgi būdami pie tā vārda piedauzās, uz ko tie arīdzan ir nolikti.
ndi “Mwala wopunthwitsa anthu ndiponso thanthwe limene limagwetsa anthu.” Iwo amapunthwa chifukwa samvera uthenga, pakuti ichi ndiye chinali chifuniro cha Mulungu pa iwo.
9 Bet jūs esat izredzēta tauta, ķēniņu priesterība, svēta cilts, Dieva īpaši ļaudis; ka jums būs pasludināt Tā tikumus, kas jūs aicinājis no tumsības pie Savas brīnišķās gaismas,
Koma inu ndinu anthu osankhidwa ndi Mulungu, ansembe achifumu, mtundu woyera mtima, anthu ake enieni a Mulungu, munasankhidwa kuti mulalikire za ntchito zamphamvu za Iye amene anakuyitanani kuti mutuluke mu mdima ndi kulowa mʼkuwunika kwake kodabwitsa.
10 Jūs, kas citkārt nebijāt Dieva ļaudis, bet tagad esat Dieva ļaudis, kas citkārt nebijāt apžēloti, bet tagad esat apžēloti.
Kale simunali anthu ake, koma tsopano ndinu anthu a Mulungu. Kale simunalandire chifundo, koma tsopano mwalandira chifundo.
11 Mīļie, es jūs pamācu kā piemājotājus un svešiniekus, ka jums būs noturēties no miesīgām kārībām, kas pret dvēseli karo,
Okondedwa, ndikukupemphani, ngati alendo pansi pano, pewani zilakolako za uchimo, zimene zimachita nkhondo ndi moyo wanu.
12 Un ka jūs dzīvojiet godīgi starp tiem pagāniem, lai kurās lietās tie jūs aprunā kā ļaundarītājus, tie to labo darbu dēļ, ko tie pie jums redz, Dievu pagodina tai piemeklēšanas dienā.
Khalani moyo wabwino pakati pa anthu osapembedza kuti ngakhale atakusinjirirani kuti mumachita zoyipa, iwowo akaona ntchito zanu zabwino, adzalemekeza Mulungu pa tsiku lomwe Iye adzatiyendere.
13 Tad esiet ikvienai cilvēku kārtībai paklausīgi Tā Kunga dēļ: gan ķēniņam, kā tādam, kas pār visiem ir iecelts,
Gonjerani maulamuliro onse chifukwa cha Ambuye. Kaya ndi mfumu, imvereni chifukwa ili ndi ulamuliro waukulu,
14 Gan valdniekiem, kā tādiem, kas no viņa ir sūtīti par atriebšanu ļaundarītājiem, bet par slavu laba darītājiem.
kaya ndi mabwanamkubwa, pakuti watumidwa ndi mfumu kuti alange onse amene amachita zoyipa ndi kuyamikira onse amene amachita zabwino.
15 Jo tāds ir Dieva prāts, ka jūs labu darīdami, muti aizbāžat neprātīgu cilvēku nezināšanai,
Pakuti Mulungu akufuna kuti pochita ntchito zabwino muthetse kuyankhula mosazindikira ndi mopusa.
16 Kā svabadnieki, un ne tā kā jums svabadība būtu par ļaunuma apsegu, bet tā kā Dieva kalpi.
Mukhale monga mfulu, koma musagwiritse ntchito ufulu wanuwo ngati chophimbira zoyipa; mukhale monga atumiki a Mulungu.
17 Turiet visus godā; mīlējiet brāļu draudzību; bīstaties Dievu, godājiet ķēniņu.
Chitirani ulemu aliyense, kondani abale okhulupirira, wopani Mulungu, ndipo chitirani mfumu ulemu.
18 Jūs kalpi, esiet paklausīgi tiem kungiem iekš visas bijāšanas, ne vien tiem labiem un lēniem, bet arī tiem bargiem.
Inu akapolo, gonjerani ambuye anu ndi kuwachitira ulemu, osati kwa iwo okha amene ndi abwino ndi omvetsa zinthu, komanso kwa amene ndi ankhanza.
19 Jo tā ir žēlastība, ja, kas Dievu apzinādamies, grūtumu panes netaisnību ciezdams.
Pakuti ndi chinthu chokoma ngati munthu apirira mu zowawa zimene sizinamuyenera chifukwa chodziwa kuti Mulungu alipo.
20 Jo kāda slava ir šī, ja jūs apgrēkodamies topat pliķēti un panesat? Bet ja jūs labu darīdami ciešat un panesat, tā ir žēlastība pie Dieva.
Kodi pali choti akuyamikireni ngati mupirira pomenyedwa chifukwa choti mwalakwa? Koma ngati mumva zowawa chifukwa chochita zabwino ndi kupirira, mwachita choyamikika pamaso pa Mulungu.
21 Jo uz to jūs esat aicināti, kā arī Kristus priekš jums ir cietis un jums priekšzīmi pametis, ka jums būs pakaļ iet Viņa pēdām:
Munayitanidwa kudzachita zimenezi, chifukwa Khristu anamva zowawa chifukwa cha inu, anakusiyirani chitsanzo, kuti inu mutsatire mʼmapazi ake.
22 Tas grēkus nav darījis, nedz viltība ir atrasta Viņa mutē,
“Iye sanachite tchimo kapena kunena bodza.”
23 Tas lamāts neatlamāja un ciezdams neļaunojās, bet nodeva to Tam, kas taisni tiesā;
Pamene anthu ankamuchita chipongwe, Iye sanabwezere chipongwe, pamene Iye ankamva zowawa, sanaopseze. Mʼmalo mwake, anadzipereka kwa Mulungu amene amaweruza molungama.
24 Tas mūsu grēkus Pats ir nesis Savā miesā pie tā koka, ka mēs, no grēkiem vaļā tikuši, taisnībai dzīvotu; caur Viņa brūcēm jūs esat dziedināti.
Iye mwini anasenza machimo athu mʼthupi lake pa mtanda, kuti ife tife kutchimo ndi kukhala ndi moyo potsata chilungamo, ndipo ndi mabala ake munachiritsidwa.
25 Jo jūs bijāt tā kā avis, kas maldās, bet tagad jūs esat atgriezti pie savu dvēseļu gana un bīskapa.
Pakuti munali monga nkhosa zosochera, koma tsopano mwabwerera kwa mʼbusa ndi woyangʼanira miyoyo yanu.

< Pēteŗa 1. Vēstule 2 >