< Pirmā Laiku 22 >

1 Un Dāvids sacīja: šeitan būs būt Dieva Tā Kunga namam, un še būs būt dedzināmo upuru altārim priekš Israēla.
Ndipo Davide anati, “Nyumba ya Yehova Mulungu idzakhala pano, ndiponso guwa lansembe zopsereza za Israeli.”
2 Un Dāvids pavēlēja sapulcināt svešiniekus, kas bija Israēla zemē, un viņš saderēja akmeņu cirtējus, apcirst akmeņus Dieva nama būvei.
Choncho Davide analamula kuti asonkhanitse alendo onse amene amakhala mu Israeli ndipo kuchokera pakati pawo anasankha amisiri a miyala kuti aseme miyala yomangira nyumba ya Mulungu.
3 Un Dāvids sakrāja daudz dzelzs priekš naglām pie vārtu durvīm un klamburiem un tik daudz vara, ka nebija sverams,
Ndipo anapereka zitsulo zambiri zopangira misomali ya zitseko za pa zipata ndi zolumikiza zake. Anaperekanso mkuwa wochuluka wokanika kuwuyeza.
4 Un ciedru koku, ka nebija skaitāmi, jo Sidonieši un Tirieši veda ciedru kokus Dāvidam lielā pulkā.
Iye anaperekanso mitengo yambiri ya mkungudza, yosawerengeka, pakuti anthu a ku Sidoni ndi a ku Turo anabweretsa yambiri kwa Davide.
5 Un Dāvids sacīja: mans dēls Salamans ir jauns un mazs, un tam namam, kas Tam Kungam jātaisa būs jo lielam būt par slavu un godu visās zemēs, tāpēc es viņam sagādāšu krājumu. Tā Dāvids sakrāja lielu krājumu, pirms nomira.
Davide anati, “Mwana wanga Solomoni ndi wamngʼono ndipo sadziwa zambiri. Koma nyumba yomwe timangire Yehova iyenera kukhala yaulemerero, yotchuka ndi yokongola pamaso pa anthu a mitundu yonse. Choncho ndikonzekeratu zambiri.” Motero Davide anayikonzekera kwambiri asanamwalire.
6 Tad viņš aicināja savu dēlu Salamanu un tam pavēlēja namu celt Tam Kungam, Israēla Dievam.
Tsono iye anayitana Solomoni mwana wake ndipo anamulamula kuti adzamangire nyumba Yehova Mulungu wa Israeli.
7 Un Dāvids sacīja uz Salamanu: mans dēls, man gan bija prātā, celt namu Tā Kunga, sava Dieva, vārdam.
Davide anati kwa Solomoni, “Mwana wanga, ine ndinali ndi maganizo oti ndimangire nyumba Dzina la Yehova Mulungu wanga.
8 Bet Tā Kunga vārds uz mani notika tā: tu esi izlējis daudz asinis, jo tu esi vedis lielus karus; tev nebūs manam vārdam celt namu, jo tu esi izlējis daudz asinis virs zemes manā priekšā.
Koma Yehova anandiyankhula kuti, ‘Iwe wapha anthu ambiri ndiponso wachita nkhondo zambiri. Sumangira dzina langa nyumba chifukwa wapha anthu ambiri pa dziko lapansi pamaso panga.
9 Redzi, tas dēls, kas tev dzims, būs miera vīrs, jo es viņam došu mieru no visiem viņa ienaidniekiem visapkārt, jo Salamans (miera vīrs) būs viņa vārds, un viņa laikā Israēlim es došu mieru un dusu.
Koma udzabala mwana wamwamuna amene adzakhala munthu wamtendere ndi wabata ndipo ndidzamupatsa mpumulo kuchokera kwa adani ake onse a mbali zonse. Dzina lake adzatchedwa Solomoni ndipo Ine ndidzapereka mtendere ndi bata kwa Israeli pa nthawi ya ulamuliro wake.
10 Tas manam vārdam cels namu un tas man būs par dēlu, un es tam būšu par tēvu, un es apstiprināšu viņa valstības krēslu pār Israēli mūžīgi.
Iye ndiye adzandimangire nyumba. Adzakhala mwana wanga ndipo Ine ndidzakhala abambo ake. Ndipo ndidzakhazikitsa mpando wake waufumu mʼdziko la Israeli mpaka muyaya.’”
11 Nu tad, mans dēls, Tas Kungs būs ar tevi un tev labi izdosies, ka tu uzcel Tam Kungam, savam Dievam, namu, kā viņš par tevi runājis.
“Tsopano mwana wanga, Yehova akhale nawe ndipo upambane ndi kumanga Nyumba ya Yehova Mulungu wako, monga momwe Iye ananenera kuti udzatero.
12 Un Tas Kungs tev dos gudrību un saprašanu un tevi cels pār Israēli, turēt Tā Kunga, sava Dieva, bauslību.
Yehova akupatse nzeru ndi kumvetsetsa pamene Iye adzakuyika kukhala wolamulira Israeli, kuti udzasunge malamulo a Yehova Mulungu wako.
13 Tad tev labi izdosies, kad tu turēsi un darīsi tos likumus un tās tiesas, ko Tas Kungs Mozum pavēlējis priekš Israēla. Ņemies drošu sirdi, nebīsties un nebaiļojies.
Ndipo udzapambana ngati udzamvera mosamala malangizo ndi malamulo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kudzera mwa Mose. Khala wamphamvu ndi wolimba mtima. Usachite mantha kapena kutaya mtima.
14 Un redzi, es esmu rūpējies un sakrājis priekš Tā Kunga nama simt tūkstoš talentus zelta un tūkstoš reiz tūkstoš talentus sudraba, un varu un dzelzi bez svara, jo tā ir ļoti daudz; ir kokus un akmeņus es esmu sakrājis; tu vari vēl gādāt klāt.
“Ine movutikira kwambiri ndapereka ku Nyumba ya Mulungu matani 3,400 agolide, matani 34,000 asiliva, ndiponso mkuwa ndi chitsulo, matabwa ndi miyala. Ndipo iwe utha kuwonjezerapo pa zimenezi.
15 Tev arī ir pulks strādnieku, akmeņu cirtēju un amatnieku pie akmeņiem un kokiem un ļaudis, mācīti uz visādu darbu.
Iwe uli ndi antchito ambiri: osema miyala, amisiri a miyala, ndi amisiri a matabwa, komanso anthu ambiri aluso la ntchito zosiyanasiyana,
16 Zelta, sudraba un vara un dzelzs ir neizskaitāms pulks. Celies un taisi, un lai Tas Kungs ir ar tevi.
zagolide ndi zasiliva, zamkuwa, zazitsulo, amisiri osawerengeka. Tsopano yamba ntchito, ndipo Yehova akhale nawe.”
17 Un Dāvids pavēlēja visiem Israēla virsniekiem, palīdzēt viņa dēlam Salamanam:
Tsono Davide analamula atsogoleri onse a Israeli kuti athandize Solomoni mwana wake.
18 Vai Tas Kungs, jūsu Dievs, nav ar jums, un jums nav devis mieru visapkārt? Jo viņš tās zemes iedzīvotājus ir devis manā rokā, un šī zeme ir pārvarēta Tā Kunga un viņa ļaužu priekšā.
Iye anawawuza kuti, “Kodi Yehova Mulungu, sali nanu? Ndipo Iye siwakupatsani mpumulo mbali zonse? Pakuti Iyeyo wapereka eni nthaka kwa inu ndipo dziko lili pa ulamuliro wa Yehova ndi anthu ake.
19 Tad nu dzenaties ar savu sirdi un ar savu dvēseli meklēt To Kungu, savu Dievu, un ceļaties un uztaisiet Dieva, Tā Kunga, svēto vietu, ka Tā Kunga derības šķirstu un svētos Dieva traukus var ienest šai namā, kas taps uztaisīts Tā Kunga vārdam.
Tsono perekani mtima wanu ndi moyo wanu kufunafuna Yehova Mulungu wanu. Yambani kumanga malo opatulika a Yehova Mulungu, kuti mubweretse Bokosi la Chipangano la Yehova ndi zinthu zopatulika za Mulungu mʼNyumba ya Mulungu imene idzamangidwa chifukwa cha dzina la Yehova.”

< Pirmā Laiku 22 >