< Pirmā Laiku 16 >

1 Un tie atveda Dieva šķirstu un to nolika tai teltī, ko Dāvids tam bija uzcēlis, un upurēja dedzināmos upurus un pateicības upurus Dieva priekšā.
Iwo anabwera nalo Bokosi la Mulungu ndipo analiyika pamalo pake mʼkati mwa tenti imene Davide anayimika ndipo iwo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Mulungu.
2 Un kad Dāvids tos dedzināmos upurus un pateicības upurus bija pabeidzis, tad viņš tos ļaudis svētīja Tā Kunga Vārdā.
Davide atatsiriza kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, iye anadalitsa anthu mʼdzina la Yehova.
3 Un viņš izdalīja ikkatram no Israēla, tā vīram kā sievai, pa klaipam maizes un pa gabalam gaļas un pa mēram vīna.
Kenaka anagawira Mwisraeli aliyense, wamwamuna ndi wamkazi, aliyense buledi mmodzi, nthuli yanyama ndiponso keke yamphesa zowuma.
4 Un kādus no Levitiem viņš nolika par kalpotājiem priekš Tā Kunga šķirsta, godāt, teikt un slavēt To Kungu, Israēla Dievu.
Iye anasankha Alevi ena kuti azitumikira pamene panali Bokosi la Yehova, kuti azipemphera, azithokoza ndi kulemekeza Yehova Mulungu wa Israeli.
5 Asafs bija par virsnieku un otrs pēc viņa Zaharija; Jeīls, Zemiramots, Jeķiēls un Matitija un Elijabs un Benaja un ObedEdoms un Jeīels ar spēlēm, somastabulēm un koklēm, un Asafs skandināja ar pulkstenīšiem.
Mtsogoleri wawo anali Asafu, wachiwiri anali Zekariya, kenaka Yeiyeli, Semiramoti, Yehieli, Matitiya, Eliabu, Benaya, Obedi-Edomu ndi Yeiyeli. Iwo amayimba azeze ndi apangwe, Asafu amayimba ziwaya za malipenga,
6 Un Benaja un Jeaziēls, tie priesteri, pūta vienmēr trumetes Dieva derības šķirsta priekšā.
ndipo ansembe Benaya ndi Yahazieli amawomba malipenga nthawi zonse pamaso pa Bokosi la Chipangano la Mulungu.
7 Tai dienā Dāvids pirmo reiz deva šo dziesmu, To Kungu slavēt, caur Asafu un viņa brāļiem:
Tsiku limeneli Davide anayamba nʼkusankha Asafu ndi anzake kuti ndiwo apereke nyimbo iyi ya matamando kwa Yehova:
8 Teiciet To Kungu, piesauciet Viņa vārdu, dariet zināmus starp tautām Viņa darbus.
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikani za ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu.
9 Dziedājiet Viņam, slavējiet To ar dziesmām, pārdomājiet visus Viņa brīnumus.
Imbirani Iye, muyimbireni nyimbo zamatamando; nenani za ntchito zake zonse zodabwitsa.
10 Slavējiet viņa svēto vārdu, lai sirds priecājās tiem, kas To Kungu meklē.
Nyadirani dzina lake loyera; ikondwere mitima ya iwo akufunafuna Yehova.
11 Vaicājiet pēc Tā Kunga un pēc Viņa stipruma, meklējiet Viņa vaigu bez mitēšanās.
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi zonse.
12 Pieminiet Viņa brīnumus, ko Viņš darījis, Viņa brīnuma zīmes un Viņa mutes tiesas.
Kumbukirani ntchito zodabwitsa wazichita, zozizwitsa zake, ndi kuweruza kwa mʼkamwa mwake,
13 Tu, Israēl, Viņa kalpa dzimums, jūs Jēkaba bērni, Dieva izredzētie.
inu zidzukulu za Israeli mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhidwa ake.
14 Viņš ir Tas Kungs, mūsu Dievs, Viņa tiesas iet pār visu zemi.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; chiweruzo chake chili pa dziko lonse lapansi.
15 Pieminiet mūžīgi Viņa derību, to vārdu, ko Viņš iecēlis tūkstošiem dzimumiem,
Iye amakumbukira pangano lake nthawi zonse, mawu amene Iye analamula, kwa mibado miyandamiyanda,
16 Ko Viņš derējis ar Ābrahāmu un ko zvērējis Īzakam.
pangano limene anachita ndi Abrahamu, lonjezo limene analumbira kwa Isake.
17 To Viņš arī Jēkabam iecēlis par likumu un Israēlim par mūžīgu derību,
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga lamulo, kwa Israeli monga pangano lamuyaya.
18 Sacīdams: tev Es došu Kanaāna zemi, jūsu mantības daļu; -
“Kwa iwe, ine ndidzapereka dziko la Kanaani monga cholowa chimene udzachilandira.”
19 Kad jūs bijāt mazs pulciņš, ne daudz, un svešinieki iekš tās.
Ali anthu owerengeka, ochepa ndithu, komanso alendo mʼdzikomo,
20 Un tie staigāja no vienas tautas pie otras, un no vienas valsts pie citiem ļaudīm.
iwo anayendayenda kuchoka ku mtundu wina kupita ku mtundu wina, ku ufumu wina kupita ku ufumu wina.
21 Viņš nekam neļāva tos spaidīt, Viņš arī ķēniņus pārmācīja viņu dēļ.
Iye sanalole munthu aliyense kuti awapondereze; chifukwa cha iwo, Iye anadzudzula mafumu:
22 Neaizskariet Manus svaidītos, un nedariet ļauna Maniem praviešiem.
“Musakhudze odzozedwa anga; musawachitire choyipa aneneri anga.”
23 Dziedājiet Tam Kungam, visa zeme, sludinājiet ikdienas Viņa pestīšanu.
Imbirani Yehova, dziko lonse lapansi; lalikani za chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
24 Teiciet pagānu starpā Viņa godu, visu tautu starpā Viņa brīnumus.
Lengezani za ulemerero wake kwa mitundu yonse, ntchito zake zonse zodabwitsa kwa anthu onse.
25 Jo Tas Kungs ir liels un ļoti slavējams un bijājams pār visiem dieviem.
Pakuti Yehova ndi wamkulu ndi woyenera kwambiri kumutamanda; Iyeyo ayenera kuopedwa kuposa milungu yonse.
26 Jo visi pagānu dievi ir elki, bet Tas Kungs debesis radījis.
Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano wopanda pake, koma Yehova analenga kumwamba.
27 Augstība un gods ir Viņa priekšā, spēks un līksmība ir Viņa vietā.
Ulemerero ndi ufumu zili pamaso pake; mphamvu ndi chimwemwe zili pa malo pokhala Iye.
28 Dodiet Tam Kungam, jūs ļaužu tautas, dodiet Tam Kungam godu un spēku,
Perekani kwa Yehova, Inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu,
29 Dodiet Tam Kungam Viņa vārda godu, atnesiet dāvanas un nāciet priekš Viņa vaiga, pielūdziet To Kungu svētā glītumā.
perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake. Bweretsani chopereka ndipo mufike pamaso pake; pembedzani Yehova mu ulemerero wachiyero chake.
30 Bīstaties priekš Viņa, visa pasaule; tiešām zeme stāv un nekustās.
Njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi! Dziko linakhazikika kolimba; silingasunthidwe.
31 Lai debess priecājās un lai zeme līksmojās, un lai saka tautu starpā: Tas Kungs ir ķēniņš.
Zakumwamba zisangalale, dziko lapansi likondwere; anene anthu a mitundu ina, “Yehova ndi mfumu!”
32 Lai jūra kauc un viss, kas iekš tās ir, lai lauki līksmojās ar visu, kas tur virsū.
Nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo; minda ikondwere, ndi zonse zili mʼmenemo!
33 Lai gavilē meža koki Tā Kunga priekšā, jo Tas nāk, zemi tiesāt.
Ndipo mitengo ya mʼnkhalango idzayimba, idzayimba chifukwa cha chimwemwe pamaso pa Yehova, pakuti akubwera kudzaweruza dziko lapansi.
34 Teiciet To Kungu, jo Viņš ir labs, un Viņa žēlastība paliek mūžīgi.
Yamikani Yehova, pakuti Iye ndi wabwino; chikondi chake chikhala mpaka muyaya.
35 Un sakāt: atpestī mūs, Dievs, mūsu Pestītājs, un sapulcini mūs un izglāb mūs no pagāniem, ka teicam Tavu svēto vārdu un Tevi augsti slavējam.
Fuwulani kuti, “Tipulumutseni, Inu Mulungu wa chipulumutso chathu, mutisonkhanitse ndipo mutipulumutse kwa anthu a mitundu ina, kuti tiyamike dzina lanu loyera, kuti tikutamandeni.”
36 Slavēts lai ir Tas Kungs, Israēla Dievs, mūžīgi mūžam, un visi ļaudis lai saka: Āmen, un lai slavē To Kungu. -
Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli, kuyambira muyaya mpaka muyaya. Ndipo anthu onse anati, “Ameni” ndipo “Tikutamandani Yehova.”
37 Tā viņš tur Tā Kunga derības šķirsta priekšā lika palikt Asafam un viņa brāļiem, vienmēr kalpot tā šķirsta priekšā, ikdienas savā kārtā,
Ndipo Davide anasiya Asafu pamodzi ndi anzake kumene kunali Bokosi la Chipangano la Yehova kuti azitumikira kumeneko nthawi zonse, monga mwa zoyenera kuchita pa tsiku lililonse.
38 Un ObedEdomam ar saviem brāļiem, - to bija sešdesmit un astoņi, ObedEdomam, Jedituna dēlam, un Osam par vārtu sargiem,
Iye anasiyanso Obedi-Edomu pamodzi ndi anzake 68 kuti azitumikira nawo pamodzi. Obedi-Edomu mwana wa Yedutuni ndi Hosa anali alonda a pa chipata.
39 Un priesterim Cadokam un viņa brāļiem, tiem priesteriem, priekš Tā Kunga dzīvokļa uz tā kalna Gibeonā,
Davide anasiya wansembe Zadoki ndi ansembe anzake ku chihema cha Yehova ku malo achipembedzo ku Gibiyoni
40 Tam Kungam upurēt dedzināmos upurus uz dedzināmo upuru altāra vienmēr, rītos un vakaros, tā kā rakstīts Tā Kunga bauslībā, ko viņš Israēlim bija pavēlējis.
kuti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa guwa lansembe nthawi zonse mmawa ndi madzulo, potsata zonse zimene zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Yehova, amene anawapereka kwa Aisraeli.
41 Un ar viņiem bija Hemans un Jedituns un tie citi izredzētie, kas ar vārdiem bija noteikti, To Kungu slavēt, ka Viņa žēlastība paliek mūžīgi.
Anthuwo anali pamodzi ndi Hemani ndi Yedutuni ndi onse amene anawasankha mowatchula dzina kuti apereke mayamiko kwa Yehova, “pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
42 Un ar šiem Hemans un Jedituns, skandināt ar trumetēm un pulkstenīšiem un ar svētu dziesmu spēlēm, bet Jedituna bērni bija par vārtu sargiem.
Hemani ndi Yedutuni anali oyangʼanira malipenga ndi ziwaya ndiponso zipangizo zina zoyimbira nyimbo zachipembedzo. Ana a Yedutuni anawayika kuti aziyangʼanira pa chipata.
43 Tā visi ļaudis nogāja ikkatrs savā namā, un Dāvids atgriezās, savu namu sveicināt.
Kenaka anthu onse anachoka, aliyense kupita kwawo. Ndipo Davide anabwerera ku nyumba kwake kukadalitsa banja lake.

< Pirmā Laiku 16 >