< Psalmorum 60 >
1 in finem his qui inmutabuntur in tituli inscriptione David in doctrina cum succendit Syriam Mesopotamiam et Syriam Soba et convertit Ioab et percussit vallem Salinarum duodecim milia Deus reppulisti nos et destruxisti nos iratus es et misertus es nobis
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
2 commovisti terram et turbasti eam sana contritiones eius quia commota est
Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
3 ostendisti populo tuo dura potasti nos vino conpunctionis
Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
4 dedisti metuentibus te significationem ut fugiant a facie arcus diapsalma ut liberentur dilecti tui
Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
5 salvum fac dextera tua et exaudi me
Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
6 Deus locutus est in sancto suo laetabor et partibor Sicima et convallem tabernaculorum metibor
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
7 meus est Galaad et meus est Manasses et Effraim fortitudo capitis mei Iuda rex meus
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
8 Moab olla spei meae in Idumeam extendam calciamentum meum mihi alienigenae subditi sunt
Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
9 quis deducet me in civitatem munitam quis deducet me usque in Idumeam
Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
10 nonne tu Deus qui reppulisti nos et non egredieris Deus in virtutibus nostris
Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
11 da nobis auxilium de tribulatione et vana salus hominis
Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
12 in Deo faciemus virtutem et ipse ad nihilum deducet tribulantes nos
Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.