< Psalmorum 135 >
1 alleluia laudate nomen Domini laudate servi Dominum
Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
2 qui statis in domo Domini in atriis domus Dei nostri
amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
3 laudate Dominum quia bonus Dominus psallite nomini eius quoniam suave
Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
4 quoniam Iacob elegit sibi Dominus Israhel in possessionem sibi
Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
5 quia ego cognovi quod magnus est Dominus et Deus noster prae omnibus diis
Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
6 omnia quae voluit Dominus fecit in caelo et in terra in mare et in omnibus abyssis
Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
7 educens nubes ab extremo terrae fulgora in pluviam fecit qui producit ventos de thesauris suis
Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
8 qui percussit primogenita Aegypti ab homine usque ad pecus
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
9 emisit signa et prodigia in medio tui Aegypte in Pharaonem et in omnes servos eius
Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
10 qui percussit gentes multas et occidit reges fortes
Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
11 Seon regem Amorreorum et Og regem Basan et omnia regna Chanaan
Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
12 et dedit terram eorum hereditatem hereditatem Israhel populo suo
ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
13 Domine nomen tuum in aeternum Domine memoriale tuum in generationem et generationem
Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
14 quia iudicabit Dominus populum suum et in servis suis deprecabitur
Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
15 simulacra gentium argentum et aurum opera manuum hominum
Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
16 os habent et non loquentur oculos habent et non videbunt
Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
17 aures habent et non audient neque enim est spiritus in ore eorum
makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
18 similes illis fiant qui faciunt ea et omnes qui sperant in eis
Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
19 domus Israhel benedicite Domino domus Aaron benedicite Domino
Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
20 domus Levi benedicite Domino qui timetis Dominum benedicite Domino
Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
21 benedictus Dominus ex Sion qui habitat in Hierusalem
Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.