< Proverbiorum 9 >
1 sapientia aedificavit sibi domum excidit columnas septem
Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
2 immolavit victimas suas miscuit vinum et proposuit mensam suam
Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
3 misit ancillas suas ut vocarent ad arcem et ad moenia civitatis
Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
4 si quis est parvulus veniat ad me et insipientibus locuta est
“Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
5 venite comedite panem meum et bibite vinum quod miscui vobis
“Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
6 relinquite infantiam et vivite et ambulate per vias prudentiae
Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
7 qui erudit derisorem ipse sibi facit iniuriam et qui arguit impium generat maculam sibi
Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.
8 noli arguere derisorem ne oderit te argue sapientem et diliget te
Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.
9 da sapienti et addetur ei sapientia doce iustum et festinabit accipere
Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.
10 principium sapientiae timor Domini et scientia sanctorum prudentia
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.
11 per me enim multiplicabuntur dies tui et addentur tibi anni vitae
Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.
12 si sapiens fueris tibimet ipsi eris si inlusor solus portabis malum
Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.
13 mulier stulta et clamosa plenaque inlecebris et nihil omnino sciens
Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.
14 sedit in foribus domus suae super sellam in excelso urbis loco
Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda,
15 ut vocaret transeuntes viam et pergentes itinere suo
kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo.
16 quis est parvulus declinet ad me et vecordi locuta est
Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati,
17 aquae furtivae dulciores sunt et panis absconditus suavior
“Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”
18 et ignoravit quod gigantes ibi sint et in profundis inferni convivae eius (Sheol )
Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol )