< Proverbiorum 4 >
1 audite filii disciplinam patris et adtendite ut sciatis prudentiam
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 donum bonum tribuam vobis legem meam ne derelinquatis
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 nam et ego filius fui patris mei tenellus et unigenitus coram matre mea
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 et docebat me atque dicebat suscipiat verba mea cor tuum custodi praecepta mea et vives
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 posside sapientiam posside prudentiam ne obliviscaris neque declines a verbis oris mei
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 ne dimittas eam et custodiet te dilige eam et servabit te
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 principium sapientiae posside sapientiam et in omni possessione tua adquire prudentiam
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 arripe illam et exaltabit te glorificaberis ab ea cum eam fueris amplexatus
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 dabit capiti tuo augmenta gratiarum et corona inclita proteget te
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 audi fili mi et suscipe verba mea ut multiplicentur tibi anni vitae
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 viam sapientiae monstravi tibi duxi te per semitas aequitatis
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 quas cum ingressus fueris non artabuntur gressus tui et currens non habebis offendiculum
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 tene disciplinam ne dimittas eam custodi illam quia ipsa est vita tua
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 ne delecteris semitis impiorum nec tibi placeat malorum via
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 fuge ab ea ne transeas per illam declina et desere eam
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 non enim dormiunt nisi malefecerint et rapitur somnus ab eis nisi subplantaverint
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 comedunt panem impietatis et vinum iniquitatis bibunt
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 iustorum autem semita quasi lux splendens procedit et crescit usque ad perfectam diem
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 via impiorum tenebrosa nesciunt ubi corruant
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 fili mi ausculta sermones meos et ad eloquia mea inclina aurem tuam
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 ne recedant ab oculis tuis custodi ea in medio cordis tui
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 vita enim sunt invenientibus ea et universae carni sanitas
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 omni custodia serva cor tuum quia ex ipso vita procedit
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 remove a te os pravum et detrahentia labia sint procul a te
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 oculi tui recta videant et palpebrae tuae praecedant gressus tuos
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 dirige semitam pedibus tuis et omnes viae tuae stabilientur
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 ne declines ad dexteram et ad sinistram averte pedem tuum a malo
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.