< Proverbiorum 15 >
1 responsio mollis frangit iram sermo durus suscitat furorem
Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo, koma mawu ozaza amautsa ukali.
2 lingua sapientium ornat scientiam os fatuorum ebullit stultitiam
Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.
3 in omni loco oculi Domini contemplantur malos et bonos
Maso a Yehova ali ponseponse, amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.
4 lingua placabilis lignum vitae quae inmoderata est conteret spiritum
Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo, koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.
5 stultus inridet disciplinam patris sui qui autem custodit increpationes astutior fiet
Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake, koma wochenjera amasamala chidzudzulo.
6 domus iusti plurima fortitudo et in fructibus impii conturbatur
Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri, zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.
7 labia sapientium disseminabunt scientiam cor stultorum dissimile erit
Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru; koma mitima ya zitsiru sitero.
8 victimae impiorum abominabiles Domino vota iustorum placabilia
Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.
9 abominatio est Domino via impii qui sequitur iustitiam diligetur ab eo
Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.
10 doctrina mala deserenti viam qui increpationes odit morietur
Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa. Odana ndi chidzudzulo adzafa.
11 infernus et perditio coram Domino quanto magis corda filiorum hominum (Sheol )
Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova, nanji mitima ya anthu! (Sheol )
12 non amat pestilens eum qui se corripit nec ad sapientes graditur
Wonyoza sakonda kudzudzulidwa; iye sapita kwa anthu anzeru.
13 cor gaudens exhilarat faciem in maerore animi deicitur spiritus
Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe, koma mtima wosweka umawawitsa moyo.
14 cor sapientis quaerit doctrinam et os stultorum pascetur inperitia
Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.
15 omnes dies pauperis mali secura mens quasi iuge convivium
Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa, koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.
16 melius est parum cum timore Domini quam thesauri magni et insatiabiles
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova, kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.
17 melius est vocare ad holera cum caritate quam ad vitulum saginatum cum odio
Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi, kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.
18 vir iracundus provocat rixas qui patiens est mitigat suscitatas
Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano, koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.
19 iter pigrorum quasi sepes spinarum via iustorum absque offendiculo
Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga, koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.
20 filius sapiens laetificat patrem et stultus homo despicit matrem suam
Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.
21 stultitia gaudium stulto et vir prudens dirigit gressus
Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru, koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.
22 dissipantur cogitationes ubi non est consilium ubi vero plures sunt consiliarii confirmantur
Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka, koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.
23 laetatur homo in sententia oris sui et sermo oportunus est optimus
Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera, ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.
24 semita vitae super eruditum ut declinet de inferno novissimo (Sheol )
Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo kuti apewe malo okhala anthu akufa. (Sheol )
25 domum superborum demolietur Dominus et firmos facit terminos viduae
Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.
26 abominatio Domini cogitationes malae et purus sermo pulcherrimus
Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova, koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.
27 conturbat domum suam qui sectatur avaritiam qui autem odit munera vivet
Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake, koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.
28 mens iusti meditatur oboedientiam os impiorum redundat malis
Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire, koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.
29 longe est Dominus ab impiis et orationes iustorum exaudiet
Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa, koma amamva pemphero la anthu olungama.
30 lux oculorum laetificat animam fama bona inpinguat ossa
Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.
31 auris quae audit increpationes vitae in medio sapientium commorabitur
Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo adzakhala pakati pa anthu anzeru.
32 qui abicit disciplinam despicit animam suam qui adquiescit increpationibus possessor est cordis
Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha, koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.
33 timor Domini disciplina sapientiae et gloriam praecedit humilitas
Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru, ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.