< Proverbiorum 12 >

1 qui diligit disciplinam diligit scientiam qui autem odit increpationes insipiens est
Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
2 qui bonus est hauriet a Domino gratiam qui autem confidit cogitationibus suis impie agit
Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
3 non roborabitur homo ex impietate et radix iustorum non commovebitur
Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
4 mulier diligens corona viro suo et putredo in ossibus eius quae confusione res dignas gerit
Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
5 cogitationes iustorum iudicia et consilia impiorum fraudulentia
Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
6 verba impiorum insidiantur sanguini os iustorum liberabit eos
Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
7 verte impios et non erunt domus autem iustorum permanebit
Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
8 doctrina sua noscetur vir qui autem vanus et excors est patebit contemptui
Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
9 melior est pauper et sufficiens sibi quam gloriosus et indigens pane
Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
10 novit iustus animas iumentorum suorum viscera autem impiorum crudelia
Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
11 qui operatur terram suam saturabitur panibus qui autem sectatur otium stultissimus est
Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
12 desiderium impii munimentum est pessimorum radix autem iustorum proficiet
Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
13 propter peccata labiorum ruina proximat malo effugiet autem iustus de angustia
Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
14 de fructu oris sui unusquisque replebitur bonis et iuxta opera manuum suarum retribuetur ei
Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
15 via stulti recta in oculis eius qui autem sapiens est audit consilia
Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
16 fatuus statim indicat iram suam qui autem dissimulat iniuriam callidus est
Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
17 qui quod novit loquitur index iustitiae est qui autem mentitur testis est fraudulentus
Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
18 est qui promittit et quasi gladio pungitur conscientiae lingua autem sapientium sanitas est
Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
19 labium veritatis firmum erit in perpetuum qui autem testis est repentinus concinnat linguam mendacii
Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
20 dolus in corde cogitantium mala qui autem ineunt pacis consilia sequitur eos gaudium
Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
21 non contristabit iustum quicquid ei acciderit impii autem replebuntur malo
Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
22 abominatio Domino labia mendacia qui autem fideliter agunt placent ei
Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
23 homo versutus celat scientiam et cor insipientium provocabit stultitiam
Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
24 manus fortium dominabitur quae autem remissa est tributis serviet
Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
25 maeror in corde viri humiliabit illud et sermone bono laetificabitur
Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
26 qui neglegit damnum propter amicum iustus est iter autem impiorum decipiet eos
Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
27 non inveniet fraudulentus lucrum et substantia hominis erit auri pretium
Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
28 in semita iustitiae vita iter autem devium ducit ad mortem
Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.

< Proverbiorum 12 >