< Job 21 >

1 respondens autem Iob dixit
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 audite quaeso sermones meos et agetis paenitentiam
“Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
3 sustinete me ut et ego loquar et post mea si videbitur verba ridete
Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
4 numquid contra hominem disputatio mea est ut merito non debeam contristari
“Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
5 adtendite me et obstupescite et superponite digitum ori vestro
Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
6 et ego quando recordatus fuero pertimesco et concutit carnem meam tremor
Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
7 quare ergo impii vivunt sublevati sunt confortatique divitiis
Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
8 semen eorum permanet coram eis propinquorum turba et nepotum in conspectu eorum
Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
9 domus eorum securae sunt et pacatae et non est virga Dei super illos
Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
10 bos eorum concepit et non abortit vacca peperit et non est privata fetu suo
Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
11 egrediuntur quasi greges parvuli eorum et infantes eorum exultant lusibus
Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
12 tenent tympanum et citharam et gaudent ad sonitum organi
Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
13 ducunt in bonis dies suos et in puncto ad inferna descendunt (Sheol h7585)
Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
14 qui dixerunt Deo recede a nobis et scientiam viarum tuarum nolumus
Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
15 quid est Omnipotens ut serviamus ei et quid nobis prodest si oraverimus illum
Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
16 verumtamen quia non sunt in manu eorum bona sua consilium impiorum longe sit a me
Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
17 quotiens lucerna impiorum extinguetur et superveniet eis inundatio et dolores dividet furoris sui
“Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
18 erunt sicut paleae ante faciem venti et sicut favilla quam turbo dispergit
Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
19 Deus servabit filiis illius dolorem patris et cum reddiderit tunc sciet
Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
20 videbunt oculi eius interfectionem suam et de furore Omnipotentis bibet
Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
21 quid enim ad eum pertinet de domo sua post se et si numerus mensuum eius dimidietur
Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
22 numquid Deum quispiam docebit scientiam qui excelsos iudicat
“Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
23 iste moritur robustus et sanus dives et felix
Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
24 viscera eius plena sunt adipe et medullis ossa illius inrigantur
thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
25 alius vero moritur in amaritudine animae absque ullis opibus
Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
26 et tamen simul in pulverem dormient et vermes operient eos
Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
27 certe novi cogitationes vestras et sententias contra me iniquas
“Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
28 dicitis enim ubi est domus principis et ubi tabernacula impiorum
Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
29 interrogate quemlibet de viatoribus et haec eadem eum intellegere cognoscetis
Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
30 quia in diem perditionis servabitur malus et ad diem furoris ducitur
Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
31 quis arguet coram eo viam eius et quae fecit quis reddet illi
Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
32 ipse ad sepulchra ducetur et in congerie mortuorum vigilabit
Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
33 dulcis fuit glareis Cocyti et post se omnem hominem trahet et ante se innumerabiles
Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
34 quomodo igitur consolamini me frustra cum responsio vestra repugnare ostensa sit veritati
“Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”

< Job 21 >