< Job 14 >

1 homo natus de muliere brevi vivens tempore repletus multis miseriis
“Munthu wobadwa mwa amayi amakhala masiku owerengeka ndipo ndi odzaza ndi mavuto okhaokha.
2 quasi flos egreditur et conteritur et fugit velut umbra et numquam in eodem statu permanet
Amaphuka ngati duwa ndipo kenaka amafota; amathawa ngati mthunzi ndipo sakhalitsa.
3 et dignum ducis super huiuscemodi aperire oculos tuos et adducere eum tecum in iudicium
Kodi munthu wotereyo nʼkumuyangʼanitsitsa? Kodi mungamubweretse pamaso panu kuti mumuzenge mlandu?
4 quis potest facere mundum de inmundo conceptum semine nonne tu qui solus es
Ndani angatulutse chabwino mʼchoyipa? Palibe ndi mmodzi yemwe!
5 breves dies hominis sunt numerus mensuum eius apud te est constituisti terminos eius qui praeterire non poterunt
Masiku a munthu ndi odziwikiratu; munakhazikitsa chiwerengero cha miyezi yake ndipo munamulembera malire amene sangathe kuwalumpha.
6 recede paululum ab eo ut quiescat donec optata veniat sicut mercennarii dies eius
Choncho Inu mumufulatire ndipo mumuleke apumule kufikira atakondwera nawo moyo ngati munthu waganyu.
7 lignum habet spem si praecisum fuerit rursum virescit et rami eius pullulant
“Mtengo uli nacho chiyembekezo: ngati wadulidwa, udzaphukiranso ndipo nthambi zake sizidzaleka kuphukira.
8 si senuerit in terra radix eius et in pulvere emortuus fuerit truncus illius
Mizu yake ingathe kukalamba mʼnthaka ndipo chitsa chake nʼkuwola pa dothi,
9 ad odorem aquae germinabit et faciet comam quasi cum primum plantatum est
koma pamene chinyontho chafika udzaphukira ndipo udzaphuka nthambi ngati mtengo wanthete.
10 homo vero cum mortuus fuerit et nudatus atque consumptus ubi quaeso est
Koma munthu amafa nayikidwa mʼmanda, amapuma mpweya wotsiriza ndipo kutha kwake nʼkomweko.
11 quomodo si recedant aquae de mari et fluvius vacuefactus arescat
Monga madzi amaphwera mʼnyanja kapena monga mtsinje umaphwera nuwuma,
12 sic homo cum dormierit non resurget donec adteratur caelum non evigilabit nec consurget de somno suo
momwemonso munthu amagona ndipo sadzukanso; mpaka zamlengalenga zidzathe, anthu sadzauka kapena kudzutsidwa ku tulo tawo.
13 quis mihi hoc tribuat ut in inferno protegas me ut abscondas me donec pertranseat furor tuus et constituas mihi tempus in quo recorderis mei (Sheol h7585)
“Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda ndi kundiphimba kuti ndisaoneke mpaka mkwiyo wanu utapita! Achikhala munandiyikira nthawi, kuti pambuyo pake mundikumbukirenso. (Sheol h7585)
14 putasne mortuus homo rursum vivet cunctis diebus quibus nunc milito expecto donec veniat inmutatio mea
Munthu akafa, kodi adzakhalanso ndi moyo? Masiku anga onse a moyo wovutikawu ndidzadikira mpaka itafika nthawi yomasulidwa.
15 vocabis et ego respondebo tibi operi manuum tuarum porriges dexteram
Inu mudzandiyitane ndipo ndidzakuyankhani; inu mudzafunitsitsa kuona cholengedwa chimene munachipanga ndi manja anu.
16 tu quidem gressus meos dinumerasti sed parces peccatis meis
Ndithudi pamenepo mudzayangʼana mayendedwe anga koma simudzalondola tchimo langa.
17 signasti quasi in sacculo delicta mea sed curasti iniquitatem meam
Zolakwa zanga zidzakulungidwa mʼthumba; inu mudzaphimba tchimo langa.
18 mons cadens defluet et saxum transfertur de loco suo
“Koma monga phiri limakokolokera ndi kuswekasweka ndipo monga thanthwe limasunthira kuchoka pa malo ake,
19 lapides excavant aquae et adluvione paulatim terra consumitur et homines ergo similiter perdes
monganso madzi oyenda amaperesera miyala ndipo madzi othamanga amakokololera nthaka, momwemonso Inu mumawononga chiyembekezo cha munthu.
20 roborasti eum paululum ut in perpetuum pertransiret inmutabis faciem eius et emittes eum
Inu mumamugonjetsa kamodzinʼkamodzi ndipo munthuyo nʼkutheratu; Inu mumasintha maonekedwe a nkhope yake ndipo mumamutaya kutali.
21 sive nobiles fuerint filii eius sive ignobiles non intelleget
Ana ake akamalemekezedwa, iyeyo sazidziwa zimenezo; akamachititsidwa manyazi iye saziona zimenezo.
22 attamen caro eius dum vivet dolebit et anima illius super semet ipso lugebit
Iye amangomva zowawa za mʼthupi lake ndipo amangodzilirira yekha mwini wakeyo.”

< Job 14 >