< Genesis 11 >
1 erat autem terra labii unius et sermonum eorundem
Nthawi imeneyo anthu onse a pa dziko lapansi ankayankhula chiyankhulo chimodzi ndipo mawu amene ankayankhula anali amodzi.
2 cumque proficiscerentur de oriente invenerunt campum in terra Sennaar et habitaverunt in eo
Pamene anthu amapita chakummawa anapeza chigwa ku dziko la Sinara nakhazikikako.
3 dixitque alter ad proximum suum venite faciamus lateres et coquamus eos igni habueruntque lateres pro saxis et bitumen pro cemento
Tsono anawuzana kuti, “Tiyeni tiwumbe njerwa ndi kuziwotcha bwinobwino.” Tsono mʼmalo mwa miyala anagwiritsa ntchito njerwa zowotcha, ndipo mʼmalo mwa matope anagwiritsa ntchito phula.
4 et dixerunt venite faciamus nobis civitatem et turrem cuius culmen pertingat ad caelum et celebremus nomen nostrum antequam dividamur in universas terras
Kenaka anati, “Tiyeni tidzimangire mzinda wokhala ndi nsanja yoti ikafike kumwamba kuti titchuke. Kupanda kutero tibalalikana pa dziko lonse lapansi.”
5 descendit autem Dominus ut videret civitatem et turrem quam aedificabant filii Adam
Koma Yehova anatsika kudzaona mzindawo ndi nsanja imene anthu aja ankayimanga.
6 et dixit ecce unus est populus et unum labium omnibus coeperuntque hoc facere nec desistent a cogitationibus suis donec eas opere conpleant
Yehova anati, “Anthuwa ndi amodzi, ndipo ali ndi chiyankhulo chimodzi. Izi akuchitazi nʼchiyambi chabe cha zomwe akufuna kukwaniritsa kuchita.
7 venite igitur descendamus et confundamus ibi linguam eorum ut non audiat unusquisque vocem proximi sui
Tiyeni titsikireko tikasokoneze chiyankhulo chawo kuti asamamvetsetsane.”
8 atque ita divisit eos Dominus ex illo loco in universas terras et cessaverunt aedificare civitatem
Choncho Yehova anabalalitsa anthu aja pa dziko lonse lapansi ndipo analeka kumanga mzindawo.
9 et idcirco vocatum est nomen eius Babel quia ibi confusum est labium universae terrae et inde dispersit eos Dominus super faciem cunctarum regionum
Nʼchifukwa chake mzindawo unatchedwa Babeli, popeza Yehova anasokoneza chiyankhulo cha anthu onse. Powachotsa kumeneko, Yehova anawabalalitsira pa dziko lonse lapansi.
10 hae generationes Sem Sem centum erat annorum quando genuit Arfaxad biennio post diluvium
Nayi mibado yochokera kwa Semu. Patapita zaka ziwiri chitatha chigumula, Semu ali ndi zaka 100, anabereka Aripakisadi.
11 vixitque Sem postquam genuit Arfaxad quingentos annos et genuit filios et filias
Atabereka Aripakisadi, Semu anakhala ndi moyo zaka 500 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
12 porro Arfaxad vixit triginta quinque annos et genuit Sale
Pamene Aripakisadi anali ndi zaka 35, anabereka Sela.
13 vixitque Arfaxad postquam genuit Sale trecentis tribus annis et genuit filios et filias
Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
14 Sale quoque vixit triginta annis et genuit Eber
Pamene Sela anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Eberi.
15 vixitque Sale postquam genuit Eber quadringentis tribus annis et genuit filios et filias
Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
16 vixit autem Eber triginta quattuor annis et genuit Faleg
Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi.
17 et vixit Eber postquam genuit Faleg quadringentis triginta annis et genuit filios et filias
Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
18 vixit quoque Faleg triginta annis et genuit Reu
Pamene Pelegi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Reu.
19 vixitque Faleg postquam genuit Reu ducentis novem annis et genuit filios et filias
Atabereka Reu, Pelegi anakhala zaka zina 209 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
20 vixit autem Reu triginta duobus annis et genuit Sarug
Pamene Reu anali ndi zaka 32, anabereka Serugi.
21 vixitque Reu postquam genuit Sarug ducentis septem annis et genuit filios et filias
Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
22 vixit vero Sarug triginta annis et genuit Nahor
Pamene Serugi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Nahori.
23 vixitque Sarug postquam genuit Nahor ducentos annos et genuit filios et filias
Atabereka Nahori, Serugi anakhala ndi moyo zaka zina 200 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
24 vixit autem Nahor viginti novem annis et genuit Thare
Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera.
25 vixitque Nahor postquam genuit Thare centum decem et novem annos et genuit filios et filias
Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
26 vixitque Thare septuaginta annis et genuit Abram et Nahor et Aran
Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.
27 hae sunt autem generationes Thare Thare genuit Abram et Nahor et Aran porro Aran genuit Loth
Nayi mibado yochokera mwa Tera. Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti.
28 mortuusque est Aran ante Thare patrem suum in terra nativitatis suae in Ur Chaldeorum
Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira.
29 duxerunt autem Abram et Nahor uxores nomen autem uxoris Abram Sarai et nomen uxoris Nahor Melcha filia Aran patris Melchae et patris Ieschae
Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani.
30 erat autem Sarai sterilis nec habebat liberos
Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.
31 tulit itaque Thare Abram filium suum et Loth filium Aran filium filii sui et Sarai nurum suam uxorem Abram filii sui et eduxit eos de Ur Chaldeorum ut irent in terram Chanaan veneruntque usque Haran et habitaverunt ibi
Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.
32 et facti sunt dies Thare ducentorum quinque annorum et mortuus est in Haran
Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.