< Deuteronomii 27 >
1 praecepit autem Moses et seniores Israhel populo dicentes custodite omne mandatum quod praecipio vobis hodie
Mose ndi akuluakulu a Israeli analamula anthu kuti, “Sungani malamulo onse amene ndikukupatsani lero lino.
2 cumque transieritis Iordanem in terram quam Dominus Deus tuus dabit tibi eriges ingentes lapides et calce levigabis eos
Mukawoloka mtsinje wa Yorodani kulowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, muyimiritse miyala ingapo ikuluikulu ndi kuyikulungiza.
3 ut possis in eis scribere omnia verba legis huius Iordane transmisso ut introeas terram quam Dominus Deus tuus dabit tibi terram lacte et melle manantem sicut iuravit patribus tuis
Mulembepo mawu onse a malamulo amenewa pamene muwoloka kulowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, dziko loyenda mkaka ndi uchi, monga momwe Yehova Mulungu wa makolo anu anakulonjezerani.
4 quando ergo transieritis Iordanem erige lapides quos ego hodie praecipio vobis in monte Hebal et levigabis calce
Ndipo mukawoloka Yorodani muyimike miyala iyi pa Phiri la Ebala monga momwe ndikukulamulirani lero lino ndipo muyikulungize.
5 et aedificabis ibi altare Domino Deo tuo de lapidibus quos ferrum non tetigit
Pamenepo mumange guwa lansembe la miyala la Yehova Mulungu wanu. Musagwiritse ntchito chida chilichonse chachitsulo pa miyalapo.
6 et de saxis informibus et inpolitis et offeres super eo holocausta Domino Deo tuo
Mumange guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu ndi miyala yakutchire ndi kuperekerapo nsembe yopsereza kwa Yehova Mulungu wanu.
7 et immolabis hostias pacificas comedesque ibi et epulaberis coram Domino Deo tuo
Muperekerepo nsembe zopereka za chiyanjano, muzidye ndi kukondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
8 et scribes super lapides omnia verba legis huius plane et lucide
Ndipo pa miyalapo mudzalembepo mawu onse a malamulo ndi malemba akuluakulu.”
9 dixeruntque Moses et sacerdotes levitici generis ad omnem Israhelem adtende et audi Israhel hodie factus es populus Domini Dei tui
Kenaka Mose ndi ansembe, amene ndi Alevi anati kwa Aisraeli onse, “Khalani chete Aisraeli inu ndipo mumvetsere! Tsopano inu ndinu anthu a Yehova Mulungu wanu.
10 audies vocem eius et facies mandata atque iustitias quas ego praecipio tibi
Muzimvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsata malamulo ake ndi malangizo ake omwe ndikukupatsani lero lino.”
11 praecepitque Moses populo in die illo dicens
Tsiku lomwelo Mose analamula anthu kuti:
12 hii stabunt ad benedicendum Domino super montem Garizim Iordane transmisso Symeon Levi Iudas Isachar Ioseph et Beniamin
Mukawoloka Yorodani, mafuko awa akayimirire pa Phiri la Gerizimu ndi kudalitsa anthu: Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Yosefe ndi Benjamini.
13 et e regione isti stabunt ad maledicendum in monte Hebal Ruben Gad et Aser Zabulon Dan et Nepthalim
Ndipo mafuko awa akayimirire pa Phiri la Ebala ndi kutchula matemberero: Rubeni, Gadi, Aseri, Zebuloni, Dani ndi Nafutali.
14 et pronuntiabunt Levitae dicentque ad omnes viros Israhel excelsa voce
Alevi adzayankhula mokweza kwa Aisraeli onse kuti:
15 maledictus homo qui facit sculptile et conflatile abominationem Domini opus manuum artificum ponetque illud in abscondito et respondebit omnis populus et dicet amen
“Ndi wotembereredwa munthu amene asema chifanizo kapena kupanga fano, ndi kuchiyika mobisa, pakuti chimenechi ndi chinthu chodetsedwa pamaso pa Yehova, ntchito za manja a anthu.”
16 maledictus qui non honorat patrem suum et matrem et dicet omnis populus amen
“Ndi wotembereredwa munthu amene sachitira ulemu abambo ake kapena amayi ake.”
17 maledictus qui transfert terminos proximi sui et dicet omnis populus amen
“Ndi wotembereredwa munthu amene amasuntha mwala wa malire wa mnzake.”
18 maledictus qui errare facit caecum in itinere et dicet omnis populus amen
“Ndi wotembereredwa munthu amene amasocheretsa munthu wosaona pa msewu.”
19 maledictus qui pervertit iudicium advenae pupilli et viduae et dicet omnis populus amen
“Ndi wotembereredwa munthu amene sachitira chilungamo mlendo, ana amasiye kapena mkazi wamasiye.”
20 maledictus qui dormit cum uxore patris sui et revelat operimentum lectuli eius et dicet omnis populus amen
“Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi mkazi wa abambo ake pakuti iye sachitira ulemu pogona pa abambo ake.”
21 maledictus qui dormit cum omni iumento et dicet omnis populus amen
“Ndi wotembereredwa munthu amene achita chigololo ndi nyama ya mtundu uli wonse.”
22 maledictus qui dormit cum sorore sua filia patris sui sive matris suae et dicet omnis populus amen
“Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi mlongo wake, mwana wamkazi wa abambo ake kapena mwana wamkazi wa amayi ake.”
23 maledictus qui dormit cum socru sua et dicet omnis populus amen
“Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi apongozi ake.”
24 maledictus qui clam percusserit proximum suum et dicet omnis populus amen
“Ndi wotembereredwa munthu amene apha mnzake mwachinsinsi.”
25 maledictus qui accipit munera ut percutiat animam sanguinis innocentis et dicet omnis populus amen
“Ndi wotembereredwa munthu amene alandira chiphuphu kuti aphe munthu wosalakwa.”
26 maledictus qui non permanet in sermonibus legis huius nec eos opere perficit et dicet omnis populus amen
“Ndi wotembereredwa aliyense amene sachita kapena sasunga mawu a malamulo awa.”