< Ii Samuelis 22 >
1 locutus est autem David Domino verba carminis huius in die qua liberavit eum Dominus de manu omnium inimicorum suorum et de manu Saul
Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.
2 et ait Dominus petra mea et robur meum et salvator meus
Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
3 Deus meus fortis meus sperabo in eum scutum meum et cornu salutis meae elevator meus et refugium meum salvator meus de iniquitate liberabis me
Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
4 laudabilem invocabo Dominum et ab inimicis meis salvus ero
“Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
5 quia circumdederunt me contritiones mortis torrentes Belial terruerunt me
“Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
6 funes inferi circumdederunt me praevenerunt me laquei mortis (Sheol )
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol )
7 in tribulatione mea invocabo Dominum et ad Deum meum clamabo et exaudiet de templo suo vocem meam et clamor meus veniet ad aures eius
“Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.
8 commota est et contremuit terra fundamenta montium concussa sunt et conquassata quoniam iratus est
“Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
9 ascendit fumus de naribus eius et ignis de ore eius voravit carbones incensi sunt ab eo
Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
10 et inclinavit caelos et descendit et caligo sub pedibus eius
Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
11 et ascendit super cherubin et volavit et lapsus est super pinnas venti
Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
12 posuit tenebras in circuitu suo latibulum cribrans aquas de nubibus caelorum
Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga.
13 prae fulgore in conspectu eius succensi sunt carbones ignis
Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi.
14 tonabit de caelis Dominus et Excelsus dabit vocem suam
Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
15 misit sagittas et dissipavit eos fulgur et consumpsit eos
Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
16 et apparuerunt effusiones maris et revelata sunt fundamenta orbis ab increpatione Domini ab inspiratione spiritus furoris eius
Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.
17 misit de excelso et adsumpsit me extraxit me de aquis multis
“Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
18 liberavit me ab inimico meo potentissimo ab his qui oderant me quoniam robustiores me erant
Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
19 praevenit me in die adflictionis meae et factus est Dominus firmamentum meum
Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
20 et eduxit me in latitudinem liberavit me quia placuit ei
Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
21 retribuet mihi Dominus secundum iustitiam meam et secundum munditiam manuum mearum reddet mihi
“Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
22 quia custodivi vias Domini et non egi impie a Deo meo
Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
23 omnia enim iudicia eius in conspectu meo et praecepta eius non amovi a me
Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake.
24 et ero perfectus cum eo et custodiam me ab iniquitate mea
Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
25 et restituet Dominus mihi secundum iustitiam meam et secundum munditiam manuum mearum in conspectu oculorum suorum
Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.
26 cum sancto sanctus eris et cum robusto perfectus
“Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
27 cum electo electus eris et cum perverso perverteris
Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
28 et populum pauperem salvum facies oculisque tuis excelsos humiliabis
Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
29 quia tu lucerna mea Domine et Domine inluminabis tenebras meas
Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
30 in te enim curram accinctus in Deo meo transiliam murum
Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
31 Deus inmaculata via eius eloquium Domini igne examinatum scutum est omnium sperantium in se
“Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye.
32 quis est deus praeter Dominum et quis fortis praeter Deum nostrum
Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
33 Deus qui accingit me fortitudine et conplanavit perfectam viam meam
Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
34 coaequans pedes meos cervis et super excelsa mea statuens me
Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
35 docens manus meas ad proelium et conponens quasi arcum aereum brachia mea
Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
36 dedisti mihi clypeum salutis tuae et mansuetudo mea multiplicavit me
Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze.
37 dilatabis gressus meos subtus me et non deficient tali mei
Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke.
38 persequar inimicos meos et conteram et non revertar donec consumam eos
“Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
39 consumam eos et confringam ut non consurgant cadent sub pedibus meis
Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
40 accinxisti me fortitudine ad proelium incurvabis resistentes mihi sub me
Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
41 inimicos meos dedisti mihi dorsum odientes me et disperdam eos
Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga.
42 clamabunt et non erit qui salvet ad Dominum et non exaudiet eos
Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
43 delebo eos ut pulverem terrae quasi lutum platearum comminuam eos atque conpingam
Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
44 salvabis me a contradictionibus populi mei custodies in caput gentium populus quem ignoro serviet mihi
“Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
45 filii alieni resistent mihi auditu auris oboedient mihi
Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.
46 filii alieni defluxerunt et contrahentur in angustiis suis
Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
47 vivit Dominus et benedictus Deus meus et exaltabitur Deus fortis salutis meae
“Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
48 Deus qui das vindictas mihi et deicis populos sub me
Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
49 qui educis me ab inimicis meis et a resistentibus mihi elevas me a viro iniquo liberabis me
amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
50 propterea confitebor tibi Domine in gentibus et nomini tuo cantabo
Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
51 magnificanti salutes regis sui et facienti misericordiam christo suo David et semini eius in sempiternum
“Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”