< Psalmorum 9 >

1 Psalmus David, in finem pro occultis filii. Confitebor tibi Domine in toto corde meo: narrabo omnia mirabilia tua.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide. Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse; ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
2 Laetabor et exultabo in te: psallam nomini tuo Altissime,
Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu; Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
3 In convertendo inimicum meum retrorsum: infirmabuntur, et peribunt a facie tua.
Adani anga amathawa, iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
4 Quoniam fecisti iudicium meum et causam meam: sedisti super thronum qui iudicas iustitiam.
Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga; Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
5 Increpasti Gentes, et periit impius: nomen eorum delesti in aeternum et in saeculum saeculi.
Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa; Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
6 Inimici defecerunt frameae in finem: et civitates eorum destruxisti. Periit memoria eorum cum sonitu:
Chiwonongeko chosatha chagwera adani, mwafafaniza mizinda yawo; ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
7 et Dominus in aeternum permanet. Paravit in iudicio thronum suum:
Yehova akulamulira kwamuyaya; wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
8 et ipse iudicabit orbem terrae in aequitate, iudicabit populos in iustitia.
Iye adzaweruza dziko mwachilungamo; adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
9 Et factus est Dominus refugium pauperi: adiutor in opportunitatibus, in tribulatione.
Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima, linga pa nthawi ya mavuto.
10 Et sperent in te qui noverunt nomen tuum: quoniam non dereliquisti quaerentes te Domine.
Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu, pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
11 Psallite Domino, qui habitat in Sion: annunciate inter Gentes studia eius:
Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni; lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
12 Quoniam requirens sanguinem eorum recordatus est: non est oblitus clamorem pauperum.
Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira; Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
13 Miserere mei Domine: vide humilitatem meam de inimicis meis.
Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira! Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
14 Qui exaltas me de portis mortis, ut annunciem omnes laudationes tuas in portis filiae Sion.
kuti ndilengeze za matamando anu pa zipata za ana aakazi a Ziyoni, kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
15 Exultabo in salutari tuo: infixae sunt Gentes in interitu, quem fecerunt. In laqueo isto, quem absconderunt, comprehensus est pes eorum.
Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba; mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
16 Cognoscetur Dominus iudicia faciens: in operibus manuum suarum comprehensus est peccator.
Yehova amadziwika ndi chilungamo chake; oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo. Higayoni. (Sela)
17 Convertantur peccatores in infernum, omnes Gentes quae obliviscuntur Deum. (Sheol h7585)
Oyipa amabwerera ku manda, mitundu yonse imene imayiwala Mulungu. (Sheol h7585)
18 Quoniam non in finem oblivio erit pauperis: patientia pauperum non peribit in finem.
Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse, kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
19 Exurge Domine, non confortetur homo: iudicentur Gentes in conspectu tuo:
Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane; mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
20 Constitue Domine legislatorem super eos: ut sciant Gentes quoniam homines sunt.
Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova; mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba. (Sela)

< Psalmorum 9 >