< Psalmorum 85 >

1 Psalmus, in finem, filiis Core. Benedixisti Domine terram tuam: avertisti captivitatem Iacob.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
2 Remisisti iniquitatem plebis tuae: operuisti omnia peccata eorum.
Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
3 Mitigasti omnem iram tuam: avertisti ab ira indignationis tuae.
Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
4 Converte nos Deus salutaris noster: et averte iram tuam a nobis.
Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
5 Numquid in aeternum irasceris nobis? aut extendes iram tuam a generatione in generationem?
Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
6 Deus tu conversus vivificabis nos: et plebs tua laetabitur in te.
Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
7 Ostende nobis Domine misericordiam tuam: et salutare tuum da nobis.
Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
8 Audiam quid loquatur in me Dominus Deus: quoniam loquetur pacem in plebem suam. Et super sanctos suos: et in eos, qui convertuntur ad cor.
Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
9 Verumtamen prope timentes eum salutare ipsius: ut inhabitet gloria in terra nostra.
Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
10 Misericordia, et veritas obviaverunt sibi: iustitia, et pax osculatae sunt.
Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
11 Veritas de terra orta est: et iustitia de caelo prospexit.
Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
12 Etenim Dominus dabit benignitatem: et terra nostra dabit fructum suum.
Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
13 Iustitia ante eum ambulabit: et ponet in via gressus suos.
Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.

< Psalmorum 85 >