< Psalmorum 78 >

1 Psalmus. Intellectus Asaph. Attendite popule meus legem meam: inclinate aurem vestram in verba oris mei.
Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
2 Aperiam in parabolis os meum: loquar propositiones ab initio.
Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
3 Quanta audivimus et cognovimus ea: et patres nostri narraverunt nobis.
zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
4 Non sunt occultata a filiis eorum, in generatione altera. Narrantes laudes Domini, et virtutes eius, et mirabilia eius quae fecit.
Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
5 Et suscitavit testimonium in Iacob: et legem posuit in Israel. Quanta mandavit patribus nostris nota facere ea filiis suis:
Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
6 ut cognoscat generatio altera. Filii qui nascentur, et exurgent, et narrabunt filiis suis,
kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
7 Ut ponant in Deo spem suam, et non obliviscantur operum Dei: et mandata eius exquirant.
Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
8 Ne fiant sicut patres eorum: generatio prava et exasperans. Generatio, quae non direxit cor suum: et non est creditus cum Deo spiritus eius.
Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
9 Filii Ephrem intendentes et mittentes arcum: conversi sunt in die belli.
Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
10 Non custodierunt testamentum Dei, et in lege eius noluerunt ambulare.
iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
11 Et obliti sunt benefactorum eius, et mirabilium eius quae ostendit eis.
Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
12 Coram patribus eorum fecit mirabilia in terra Aegypti, in campo Taneos.
Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
13 Interrupit mare, et perduxit eos: et statuit aquas quasi in utre.
Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
14 Et deduxit eos in nube diei: et tota nocte in illuminatione ignis.
Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
15 Interrupit petram in eremo: et adaquavit eos velut in abysso multa.
Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
16 Et eduxit aquam de petra: et deduxit tamquam flumina aquas.
Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
17 Et apposuerunt adhuc peccare ei: in iram excitaverunt Excelsum in inaquoso.
Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
18 Et tentaverunt Deum in cordibus suis: ut peterent escas animabus suis.
Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
19 Et male locuti sunt de Deo: dixerunt: Numquid poterit Deus parare mensam in deserto?
Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
20 Quoniam percussit petram, et fluxerunt aquae, et torrentes inundaverunt. Numquid et panem poterit dare, aut parare mensam populo suo?
Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
21 Ideo audivit Dominus, et distulit: et ignis accensus est in Iacob, et ira ascendit in Israel:
Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
22 Quia non crediderunt in Deo, nec speraverunt in salutari eius:
pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
23 Et mandavit nubibus desuper, et ianuas caeli aperuit.
Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
24 Et pluit illis manna ad manducandum, et panem caeli dedit eis.
anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
25 Panem angelorum manducavit homo: cibaria misit eis in abundantia.
Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
26 Transtulit Austrum de caelo: et induxit in virtute sua Africum.
Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
27 Et pluit super eos sicut pulverem carnes, et sicut arenam maris volatilia pennata.
Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
28 Et ceciderunt in medio castrorum eorum: circa tabernacula eorum.
Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
29 Et manducaverunt et saturati sunt nimis, et desiderium eorum attulit eis:
Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
30 non sunt fraudati a desiderio suo. Adhuc escae eorum erant in ore ipsorum,
Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
31 et ira Dei ascendit super eos. Et occidit pingues eorum, et electos Israel impedivit.
mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
32 In omnibus his peccaverunt adhuc: et non crediderunt in mirabilibus eius.
Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
33 Et defecerunt in vanitate dies eorum: et anni eorum cum festinatione.
Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
34 Cum occideret eos, quaerebant eum: et revertebantur, et diluculo veniebant ad eum.
Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
35 Et rememorati sunt quia Deus adiutor est eorum: et Deus excelsus redemptor eorum est.
Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
36 Et dilexerunt eum in ore suo, et lingua sua mentiti sunt ei:
Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
37 Cor autem eorum non erat rectum cum eo: nec fideles habiti sunt in testamento eius.
Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
38 Ipse autem est misericors, et propitius fiet peccatis eorum: et non disperdet eos. Et abundavit ut averteret iram suam: et non accendit omnem iram suam:
Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
39 Et recordatus est quia caro sunt: spiritus vadens, et non rediens.
Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
40 Quoties exacerbaverunt eum in deserto, in iram concitaverunt eum in inaquoso?
Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
41 Et conversi sunt, et tentaverunt Deum: et sanctum Israel exacerbaverunt.
Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
42 Non sunt recordati manus eius, die qua redemit eos de manu tribulantis,
Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
43 Sicut posuit in Aegypto signa sua, et prodigia sua in campo Taneos.
tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
44 Et convertit in sanguinem flumina eorum, et imbres eorum, ne biberent.
Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
45 Misit in eos cynomyiam, et comedit eos: et ranam, et disperdidit eos.
Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
46 Et dedit aerugini fructus eorum: et labores eorum locustae.
Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
47 Et occidit in grandine vineas eorum: et moros eorum in pruina.
Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
48 Et tradidit grandini iumenta eorum: et possessionem eorum igni.
Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
49 Misit in eos iram indignationis suae: indignationem, et iram, et tribulationem: immissiones per angelos malos.
Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
50 Viam fecit semitae irae suae, non pepercit a morte animabus eorum: et iumenta eorum in morte conclusit.
Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
51 Et percussit omne primogenitum in terra Aegypti: primitias omnis laboris eorum in tabernaculis Cham.
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
52 Et abstulit sicut oves populum suum: et perduxit eos tamquam gregem in deserto.
Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
53 Et eduxit eos in spe, et non timuerunt: et inimicos eorum operuit mare.
Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
54 Et induxit eos in montem sanctificationis suae, montem, quem acquisivit dextera eius. Et eiecit a facie eorum Gentes: et sorte divisit eis terram in funiculo distributionis.
Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
55 Et habitare fecit in tabernaculis eorum tribus Israel.
Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
56 Et tentaverunt, et exacerbaverunt Deum excelsum: et testimonia eius non custodierunt.
Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
57 Et averterunt se, et non servaverunt pactum: quemadmodum patres eorum, conversi sunt in arcum pravum.
Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
58 In iram concitaverunt eum in collibus suis: et in sculptilibus suis ad aemulationem eum provocaverunt.
Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
59 Audivit Deus, et sprevit: et ad nihilum redegit valde Israel.
Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
60 Et repulit tabernaculum Silo, tabernaculum suum, ubi habitavit in hominibus.
Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
61 Et tradidit in captivitatem virtutem eorum: et pulchritudinem eorum in manus inimici.
Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
62 Et conclusit in gladio populum suum: et hereditatem suam sprevit.
Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
63 Iuvenes eorum comedit ignis: et virgines eorum non sunt lamentatae.
Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
64 Sacerdotes eorum in gladio ceciderunt: et viduae eorum non plorabantur.
ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
65 Et excitatus est tamquam dormiens Dominus, tamquam potens crapulatus a vino.
Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
66 Et percussit inimicos suos in posteriora: opprobrium sempiternum dedit illis.
Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
67 Et repulit tabernaculum Ioseph: et tribum Ephraim non elegit:
Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
68 Sed elegit tribum Iuda, montem Sion quem dilexit.
Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
69 Et aedificavit sicut unicornium sanctificium suum in terra, quam fundavit in saecula.
Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
70 Et elegit David servum suum, et sustulit eum de gregibus ovium: de post foetantes accepit eum.
Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
71 Pascere Iacob servum suum, et Israel hereditatem suam:
kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
72 Et pavit eos in innocentia cordis sui: et in intellectibus manuum suarum deduxit eos.
Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.

< Psalmorum 78 >