< Psalmorum 37 >

1 Psalmus David. Noli aemulari in malignantibus: neque zelaveris facientes iniquitatem.
Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
2 Quoniam tamquam foenum velociter arescent: quemadmodum olera herbarum cito decident.
pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
3 Spera in Domino, et fac bonitatem: et inhabita terram, et pasceris in divitiis eius.
Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
4 Delectare in Domino: et dabit tibi petitiones cordis tui.
Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
5 Revela Domino viam tuam, et spera in eo: et ipse faciet.
Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
6 Et educet quasi lumen iustitiam tuam: et iudicium tuum tamquam meridiem:
Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
7 subditus esto Domino, et ora eum. Noli aemulari in eo, qui prosperatur in via sua: in homine faciente iniustitias.
Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
8 Desine ab ira, et derelinque furorem: noli aemulari ut maligneris.
Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
9 Quoniam qui malignantur, exterminabuntur: sustinentes autem Dominum, ipsi hereditabunt terram.
Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
10 Et adhuc pusillum, et non erit peccator: et quaeres locum eius, et non invenies.
Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
11 Mansueti autem hereditabunt terram, et delectabuntur in multitudine pacis.
Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
12 Observabit peccator iustum: et stridebit super eum dentibus suis.
Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
13 Dominus autem irridebit eum: quoniam prospicit quod veniet dies eius.
koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
14 Gladium evaginaverunt peccatores: intenderunt arcum suum. Ut decipiant pauperem et inopem: ut trucident rectos corde.
Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
15 Gladius eorum intret in corda ipsorum: et arcus eorum confringatur.
Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
16 Melius est modicum iusto, super divitias peccatorum multas.
Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
17 Quoniam brachia peccatorum conterentur: confirmat autem iustos Dominus.
pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
18 Novit Dominus dies immaculatorum: et hereditas eorum in aeternum erit.
Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
19 Non confundentur in tempore malo, et in diebus famis saturabuntur:
Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
20 quia peccatores peribunt. Inimici vero Domini mox ut honorificati fuerint et exaltati: deficientes, quemadmodum fumus deficient.
Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
21 Mutuabitur peccator, et non solvet: iustus autem miseretur et retribuet.
Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
22 Quia benedicentes ei hereditabunt terram: maledicentes autem ei disperibunt.
Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
23 Apud Dominum gressus hominis dirigentur: et viam eius volet.
Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
24 Cum ceciderit, non collidetur: quia Dominus supponit manum suam.
ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
25 Iunior fui, etenim senui: et non vidi iustum derelictum, nec semen eius quaerens panem.
Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
26 Tota die miseretur et commodat: et semen illius in benedictione erit.
Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
27 Declina a malo, et fac bonum: et inhabita in saeculum saeculi.
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
28 Quia Dominus amat iudicium, et non derelinquet sanctos suos: in aeternum conservabuntur. Iniusti punientur: et semen impiorum peribit.
Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
29 Iusti autem hereditabunt terram: et inhabitabunt in saeculum saeculi super eam.
olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
30 Os iusti meditabitur sapientiam, et lingua eius loquetur iudicium.
Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
31 Lex Dei eius in corde ipsius: et non supplantabuntur gressus eius.
Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
32 Considerat peccator iustum: et quaerit mortificare eum.
Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
33 Dominus autem non derelinquet eum in manibus eius: nec damnabit eum cum iudicabitur illi.
koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
34 Expecta Dominum, et custodi viam eius: et exaltabit te ut hereditate capias terram: cum perierint peccatores videbis.
Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
35 Vidi impium superexaltatum, et elevatum sicut cedros Libani.
Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
36 Et transivi, et ecce non erat: quaesivi eum, et non est inventus locus eius.
Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
37 Custodi innocentiam, et vide aequitatem: quoniam sunt reliquiae homini pacifico.
Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
38 Iniusti autem disperibunt simul: reliquiae impiorum interibunt.
Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
39 Salus autem iustorum a Domino: et protector eorum in tempore tribulationis.
Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
40 Et adiuvabit eos Dominus, et liberabit eos: et eruet eos a peccatoribus, et salvabit eos: quia speraverunt in eo.
Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.

< Psalmorum 37 >