< Psalmorum 34 >
1 Psalmus David, cum immutavit vultum suum coram Achimelech, et dimisit eum et abiit. Benedicam Dominum in omni tempore: semper laus eius in ore meo.
Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
2 In Domino laudabitur anima mea: audiant mansueti, et laetentur.
Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
3 Magnificate Dominum mecum: et exaltemus nomen eius in idipsum.
Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
4 Exquisivi Dominum, et exaudivit me: et ex omnibus tribulationibus meis eripuit me.
Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
5 Accedite ad eum, et illuminamini: et facies vestrae non confundentur.
Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
6 Iste pauper clamavit, et Dominus exaudivit eum: et de omnibus tribulationibus eius salvavit eum.
Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
7 Immittet angelus Domini in circuitu timentium eum: et eripiet eos.
Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
8 Gustate, et videte quoniam suavis est Dominus: beatus vir, qui sperat in eo.
Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
9 Timete Dominum omnes sancti eius: quoniam non est inopia timentibus eum.
Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
10 Divites eguerunt et esurierunt: inquirentes autem Dominum non minuentur omni bono.
Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
11 Venite filii, audite me: timorem Domini docebo vos.
Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
12 Quis est homo qui vult vitam: diligit dies videre bonos?
Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
13 Prohibe linguam tuam a malo: et labia tua ne loquantur dolum.
asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
14 Diverte a malo, et fac bonum: inquire pacem, et persequere eam.
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
15 Oculi Domini super iustos: et aures eius in preces eorum.
Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
16 Vultus autem Domini super facientes mala: ut perdat de terra memoriam eorum.
nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
17 Clamaverunt iusti, et Dominus exaudivit eos: et ex omnibus tribulationibus eorum liberavit eos.
Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
18 Iuxta est Dominus iis, qui tribulato sunt corde: et humiles spiritu salvabit.
Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
19 Multae tribulationes iustorum: et de omnibus his liberabit eos Dominus.
Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
20 Custodit Dominus omnia ossa eorum: unum ex his non conteretur.
Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
21 Mors peccatorum pessima: et qui oderunt iustum delinquent.
Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
22 Redimet Dominus animas servorum suorum: et non delinquent omnes qui sperant in eo.
Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.