< Psalmorum 2 >

1 Quare fremuerunt Gentes, et populi meditati sunt inania? Astiterunt reges terrae, et principes convenerunt in unum adversus Dominum, et adversus Christum eius.
Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
2 Dirumpamus vincula eorum: et proiiciamus a nobis iugum ipsorum.
Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
3 Qui habitat in caelis irridebit eos: et Dominus subsannabit eos.
Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
4 Tunc loquetur ad eos in ira sua, et in furore suo conturbabit eos.
Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
5 Ego autem constitutus sum rex ab eo super Sion montem sanctum eius, praedicans praeceptum eius.
Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
6 Dominus dixit ad me: Filius meus es tu, ego hodie genui te.
“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
7 Postula a me, et dabo tibi Gentes hereditatem tuam, et possessionem tuam terminos terrae.
Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
8 Reges eos in virga ferrea, et tamquam vas figuli confringes eos.
Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
9 Et nunc reges intelligite: erudimini qui iudicatis terram.
Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
10 Servite Domino in timore: et exultate ei cum tremore.
Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
11 Apprehendite disciplinam nequando irascatur Dominus, et pereatis de via iusta.
Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
12 Cum exarserit in brevi ira eius, beati omnes, qui confidunt in eo.
Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.

< Psalmorum 2 >