< Psalmorum 150 >

1 Alleluia. Laudate Dominum in sanctis eius: laudate eum in firmamento virtutis eius.
Tamandani Yehova. Tamandani Mulungu mʼmalo ake opatulika; mutamandeni ku thambo lake lamphamvu.
2 Laudate eum in virtutibus eius: laudate eum secundum multitudinem magnitudinis eius.
Mutamandeni chifukwa cha machitidwe ake amphamvu; mutamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana.
3 Laudate eum in sono tubae: laudate eum in psalterio, et cithara.
Mutamandeni poyimba malipenga, mutamandeni ndi pangwe ndi zeze.
4 Laudate eum in tympano, et choro: laudate eum in chordis, et organo.
Mutamandeni ndi matambolini ndi kuvina, mutamandeni ndi zingwe ndi zitoliro.
5 Laudate eum in cymbalis benesonantibus: laudate eum in cymbalis iubilationis:
Mutamandeni ndi ziwaya zolira za malipenga, mutamandeni ndi ziwaya zolira kwambiri.
6 omnis spiritus laudet Dominum. Alleluia.
Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Yehova. Tamandani Yehova.

< Psalmorum 150 >