< Psalmorum 146 >
1 Alleluia, Aggaei, et Zachariae.
Tamandani Yehova. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
2 Lauda anima mea Dominum, laudabo Dominum in vita mea: psallam Deo meo quamdiu fuero. Nolite confidere in principibus:
Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.
3 in filiis hominum, in quibus non est salus.
Musamadalire mafumu, anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.
4 Exibit spiritus eius, et revertetur in terram suam: in illa die peribunt omnes cogitationes eorum.
Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi; zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.
5 Beatus, cuius Deus Iacob adiutor eius, spes eius in Domino Deo ipsius:
Wodala ndi amene thandizo lake ndi Mulungu wa Yakobo.
6 qui fecit caelum et terram, mare, et omnia, quae in eis sunt.
Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo; Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.
7 Qui custodit veritatem in saeculum, facit iudicium iniuriam patientibus: dat escam esurientibus. Dominus solvit compeditos:
Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala. Yehova amamasula amʼndende,
8 Dominus illuminat caecos. Dominus erigit elisos, Dominus diligit iustos.
Yehova amatsekula maso anthu osaona, Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi, Yehova amakonda anthu olungama.
9 Dominus custodit advenas, pupillum et viduam suscipiet: et vias peccatorum disperdet.
Yehova amasamalira alendo ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye, koma amasokoneza njira za anthu oyipa.
10 Regnabit Dominus in saecula Deus tuus Sion, in generatione et generationem.
Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya, Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse. Tamandani Yehova.