< Psalmorum 137 >

1 Psalmus David, propter Hieremiam. Super flumina Babylonis, illic sedimus et flevimus: cum recordaremur Sion:
Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
2 In salicibus in medio eius, suspendimus organa nostra.
Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
3 Quia illic interrogaverunt nos, qui captivos duxerunt nos, verba cantionum: Et qui abduxerunt nos: Hymnum cantate nobis de canticis Sion.
pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
4 Quomodo cantabimus canticum Domini in terra aliena?
Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
5 Si oblitus fuero tui Ierusalem, oblivioni detur dextera mea.
Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
6 Adhaereat lingua mea faucibus meis, si non meminero tui: Si non proposuero Ierusalem, in principio laetitiae meae.
Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
7 Memor esto Domine filiorum Edom, in die Ierusalem: Qui dicunt: Exinanite, exinanite usque ad fundamentum in ea.
Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
8 Filia Babylonis misera: beatus, qui retribuet tibi retributionem tuam, quam retribuisti nobis.
Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
9 Beatus, qui tenebit, et allidet parvulos suos ad petram.
Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.

< Psalmorum 137 >