< Psalmorum 128 >

1 Canticum graduum. Beati omnes, qui timent Dominum, qui ambulant in viis eius.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.
2 Labores manuum tuarum quia manducabis: beatus es, et bene tibi erit.
Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
3 Uxor tua sicut vitis abundans, in lateribus domus tuae. Filii tui sicut novellae olivarum, in circuitu mensae tuae.
Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.
4 Ecce sic benedicetur homo, qui timet Dominum.
Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.
5 Benedicat tibi Dominus ex Sion: et videas bona Ierusalem omnibus diebus vitae tuae.
Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,
6 Et videas filios filiorum tuorum, pacem super Israel.
ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.

< Psalmorum 128 >