< Psalmorum 115 >

1 NON NOBIS DOMINE, NON NOBIS: sed nomini tuo da gloriam.
Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
2 Super misericordia tua, et veritate tua: nequando dicant Gentes: Ubi est Deus eorum?
Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
3 Deus autem noster in caelo: omnia quaecumque voluit, fecit.
Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
4 Simulacra gentium argentum, et aurum, opera manuum hominum.
Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
5 Os habent, et non loquentur: oculos habent, et non videbunt.
Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
6 Aures habent, et non audient: nares habent, et non odorabunt.
makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
7 Manus habent, et non palpabunt: pedes habent, et non ambulabunt: non clamabunt in gutture suo.
manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
8 Similes illis fiant qui faciunt ea: et omnes qui confidunt in eis.
Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
9 Domus Israel speravit in Domino: adiutor eorum et protector eorum est.
Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
10 Domus Aaron speravit in Domino: adiutor eorum et protector eorum est.
Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
11 Qui timent Dominum, speraverunt in Domino: adiutor eorum et protector eorum est.
Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
12 Dominus memor fuit nostri: et benedixit nobis: Benedixit domui Israel: benedixit domui Aaron.
Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
13 Benedixit omnibus, qui timent Dominum, pusillis cum maioribus.
adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
14 Adiiciat Dominus super vos: super vos, et super filios vestros.
Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
15 Benedicti vos a Domino, qui fecit caelum, et terram.
Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
16 Caelum caeli Domino: terram autem dedit filiis hominum.
Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
17 Non mortui laudabunt te Domine: neque omnes, qui descendunt in infernum. (questioned)
Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
18 Sed nos qui vivimus, benedicimus Domino, ex hoc nunc et usque in saeculum.
ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.

< Psalmorum 115 >