< Psalmorum 114 >

1 Alleluia. In exitu Israel de Aegypto, domus Iacob de populo barbaro:
Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
2 Facta est Iudaea sanctificatio eius, Israel potestas eius.
Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
3 Mare vidit, et fugit: Iordanis conversus est retrorsum.
Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
4 Montes exultaverunt ut arietes: et colles sicut agni ovium.
mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
5 Quid est tibi mare quod fugisti: et tu Iordanis, quia conversus es retrorsum?
Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
6 Montes exultastis sicut arietes, et colles sicut agni ovium?
inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
7 A facie Domini mota est terra, a facie Dei Iacob.
Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
8 Qui convertit petram in stagna aquarum, et rupem in fontes aquarum.
amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.

< Psalmorum 114 >