< Proverbiorum 7 >

1 Fili mi, custodi sermones meos, et praecepta mea reconde tibi. Fili
Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
2 serva mandata mea, et vives: et legem meam quasi pupillam oculi tui:
Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
3 liga eam in digitis tuis, scribe illam in tabulis cordis tui.
Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
4 Dic sapientiae, soror mea es: et prudentiam voca amicam tuam,
Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
5 ut custodiant te a muliere extranea, et ab aliena, quae verba sua dulcia facit.
Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
6 De fenestra enim domus meae per cancellos prospexi,
Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
7 et video parvulos, considero vecordem iuvenem,
Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
8 qui transit per plateam iuxta angulum, et prope viam domus illius, graditur
Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
9 in obscuro, advesperascente die, in noctis tenebris, et caligine.
Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
10 Et ecce occurrit illi mulier ornatu meretricio, praeparata ad decipiendas animas: garrula, et vaga,
Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
11 quietis impatiens, nec valens in domo consistere pedibus suis,
(Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
12 nunc foris, nunc in plateis, nunc iuxta angulos insidians.
Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
13 Apprehensumque deosculatur iuvenem, et procaci vultu blanditur, dicens:
Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
14 Victimas pro salute vovi, hodie reddidi vota mea.
“Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
15 idcirco egressa sum in occursum tuum, desiderans te videre, et reperi.
Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
16 Intexui funibus lectulum meum, stravi tapetibus pictis ex Aegypto.
Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
17 aspersi cubile meum myrrha, et aloe, et cinnamomo.
Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
18 Veni, inebriemur uberibus, et fruamur cupitis amplexibus, donec illucescat dies.
Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
19 non est enim vir in domo sua, abiit via longissima.
Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
20 sacculum pecuniae secum tulit: in die plenae lunae reversurus est in domum suam.
Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
21 Irretivit eum multis sermonibus, et blanditiis labiorum protraxit illum.
Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
22 Statim eam sequitur quasi bos ductus ad victimam, et quasi agnus lasciviens, et ignorans quod ad vincula stultus trahatur,
Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
23 donec transfigat sagitta iecur eius: velut si avis festinet ad laqueum, et nescit quod de periculo animae illius agitur.
mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
24 Nunc ergo fili mi, audi me, et attende verbis oris mei.
Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
25 Ne abstrahatur in viis illius mens tua: neque decipiaris semitis eius.
Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
26 multos enim vulneratos deiecit, et fortissimi quique interfecti sunt ab ea.
Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
27 Viae inferi domus eius, penetrantes in interiora mortis. (Sheol h7585)
Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol h7585)

< Proverbiorum 7 >