< Proverbiorum 4 >

1 Audite filii disciplinam patris, et attendite ut sciatis prudentiam.
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 Donum bonum tribuam vobis, legem meam ne derelinquatis.
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 Nam et ego filius fui patris mei, tenellus, et unigenitus coram matre mea:
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 et docebat me, atque dicebat: Suscipiat verba mea cor tuum, custodi praecepta mea, et vives.
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 Posside sapientiam, posside prudentiam: ne obliviscaris, neque declines a verbis oris mei.
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 Ne dimittas eam, et custodiet te: dilige eam, et conservabit te.
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 Principium sapientiae, posside sapientiam, et in omni possessione tua acquire prudentiam:
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 arripe illam, et exaltabit te: glorificaberis ab ea, cum eam fueris amplexatus.
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 dabit capiti tuo augmenta gratiarum, et corona inclyta proteget te.
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 Audi fili mi, et suscipe verba mea, ut multiplicentur tibi anni vitae.
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 Viam sapientiae monstrabo tibi, ducam te per semitas aequitatis:
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 quas cum ingressus fueris, non arctabuntur gressus tui, et currens non habebis offendiculum.
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 Tene disciplinam, ne dimittas eam: custodi illam, quia ipsa est via tua.
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 Ne delecteris in semitis impiorum, nec tibi placeat malorum via.
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 Fuge ab ea, nec transeas per illam: declina, et desere eam.
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 non enim dormiunt nisi malefecerint: et non capitur somnus ab eis nisi supplantaverint.
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 comedunt panem impietatis, et vinum iniquitatis bibunt.
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 Iustorum autem semita quasi lux splendens, procedit et crescit usque ad perfectam diem.
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 Via impiorum tenebrosa: nesciunt ubi corruant.
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 Fili mi, ausculta sermones meos, et ad eloquia mea inclina aurem tuam.
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 ne recedant ab oculis tuis, custodi ea in medio cordis tui:
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 vita enim sunt invenientibus ea, et universae carni sanitas.
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 Omni custodia serva cor tuum, quia ex ipso vita procedit.
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 Remove a te os pravum, et detrahentia labia sint procul a te.
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 Oculi tui recta videant, et palpebrae tuae praecedant gressus tuos.
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 Dirige semitam pedibus tuis, et omnes viae tuae stabilientur.
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 Ne declines ad dexteram, neque ad sinistram: averte pedem tuum a malo. vias enim, quae a dextris sunt, novit Dominus: perversae vero sunt quae a sinistris sunt. Ipse autem rectos faciet cursus tuos, itinera autem tua in pace producet.
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.

< Proverbiorum 4 >