< Proverbiorum 23 >

1 Quando sederis ut comedas cum principe, diligenter attende quae apposita sunt ante faciem tuam:
Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
2 et statue cultrum in gutture tuo, si tamen habes in potestate animam tuam,
ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
3 ne desideres de cibis eius, in quo est panis mendacii.
Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
4 Noli laborare ut diteris: sed prudentiae tuae pone modum.
Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
5 Ne erigas oculos tuos ad opes, quas non potes habere: quia facient sibi pennas quasi aquilae, et volabunt in caelum.
Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
6 Ne comedas cum homine invido, et ne desideres cibos eius:
Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
7 quoniam in similitudinem arioli, et coniectoris, aestimat quod ignorat. Comede et bibe, dicet tibi: et mens eius non est tecum.
paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
8 Cibos, quos comederas, evomes: et perdes pulchros sermones tuos.
Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
9 In auribus insipientium ne loquaris: qui despicient doctrinam eloquii tui.
Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
10 Ne attingas parvulorum terminos: et agrum pupillorum ne introeas:
Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
11 Propinquus enim illorum fortis est: et ipse iudicabit contra te causam illorum.
paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
12 Ingrediatur ad doctrinam cor tuum: et aures tuae ad verba scientiae.
Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
13 Noli subtrahere a puero disciplinam: si enim percusseris eum virga, non morietur.
Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
14 Tu virga percuties eum: et animam eius de inferno liberabis. (Sheol h7585)
Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol h7585)
15 Fili mi, si sapiens fuerit animus tuus, gaudebit tecum cor meum:
Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
16 et exultabunt renes mei, cum locuta fuerint recta labia tua.
Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
17 Non aemuletur cor tuum peccatores: sed in timore Domini esto tota die:
Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
18 quia habebis spem in novissimo, et praestolatio tua non auferetur.
Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
19 Audi fili mi, et esto sapiens: et dirige in via animum tuum.
Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
20 Noli esse in conviviis potatorum, nec in comessationibus eorum, qui carnes ad vescendum conferunt:
Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
21 quia vacantes potibus, et dantes symbola consumentur, et vestietur pannis dormitatio.
Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
22 Audi patrem tuum, qui genuit te: et ne contemnas cum senuerit mater tua.
Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
23 Veritatem eme, et noli vendere sapientiam, et doctrinam, et intelligentiam.
Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
24 Exultat gaudio pater iusti: qui sapientem genuit, laetabitur in eo.
Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25 Gaudeat pater tuus, et mater tua, et exultet quae genuit te.
Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
26 Praebe fili mi cor tuum mihi: et oculi tui vias meas custodiant.
Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
27 Fovea enim profunda est meretrix: et puteus angustus, aliena.
Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
28 Insidiatur in via quasi latro, et quos incautos viderit, interficiet.
Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
29 Cui vae? cuius patri vae? cui rixae? cui foveae? cui sine causa vulnera? cui suffusio oculorum?
Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
30 Nonne his, qui commorantur in vino, et student calicibus epotandis?
Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
31 Ne intuearis vinum quando flavescit, cum splenduerit in vitro color eius: ingreditur blande,
Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
32 sed in novissimo mordebit ut coluber, et sicut regulus venena diffundet.
Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
33 Oculi tui videbunt extraneas, et cor tuum loquetur perversa.
Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
34 Et eris sicut dormiens in medio mari, et quasi sopitus gubernator, amisso clavo:
Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
35 et dices: Verberaverunt me, sed non dolui: traxerunt me, et ego non sensi: quando evigilabo, et rursus vina reperiam?
Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”

< Proverbiorum 23 >