< Proverbiorum 12 >
1 Qui diligit disciplinam, diligit scientiam: qui autem odit increpationes, insipiens est.
Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
2 Qui bonus est, hauriet gratiam a Domino: qui autem confidit in cogitationibus suis, impie agit,
Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
3 Non roborabitur homo ex impietate: et radix iustorum non commovebitur.
Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
4 Mulier diligens, corona est viro suo: et putredo in ossibus eius, quae confusione res dignas gerit.
Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
5 Cogitationes iustorum iudicia: et consilia impiorum fraudulenta:
Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
6 Verba impiorum insidiantur sanguini: os iustorum liberabit eos.
Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
7 Verte impios, et non erunt: domus autem iustorum permanebit.
Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
8 Doctrina sua noscitur vir: qui autem vanus et excors est, patebit contemptui.
Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
9 Melior est pauper et sufficiens sibi, quam gloriosus et indigens pane.
Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
10 Novit iustus iumentorum suorum animas: viscera autem impiorum crudelia.
Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
11 Qui operatur terram suam, satiabitur panibus: qui autem sectatur otium, stultissimus est. Qui suavis est in vini morationibus, in suis munitionibus relinquit contumeliam.
Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
12 Desiderium impii monumentum est pessimorum: radix autem iustorum proficiet.
Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
13 Propter peccata labiorum ruina proximat malo: effugiet autem iustus de angustia.
Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
14 De fructu oris sui unusquisque replebitur bonis, et iuxta opera manuum suarum retribuetur ei.
Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
15 Via stulti recta in oculis eius: qui autem sapiens est, audit consilia.
Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
16 Fatuus statim indicat iram suam: qui autem dissimulat iniuriam, callidus est.
Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
17 Qui quod novit loquitur, iudex iustitiae est: qui autem mentitur, testis est fraudulentus.
Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
18 Est qui promittit, et quasi gladio pungitur conscientiae: lingua autem sapientium sanitas est.
Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
19 Labium veritatis firmum erit in perpetuum: qui autem testis est repentinus, concinnat linguam mendacii.
Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
20 Dolus in corde cogitantium mala: qui autem pacis ineunt consilia, sequitur eos gaudium.
Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
21 Non contristabit iustum quidquid ei acciderit: impii autem replebuntur malo.
Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
22 Abominatio est Domino labia mendacia: qui autem fideliter agunt, placent ei.
Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
23 Homo versatus celat scientiam: et cor insipientium provocat stultitiam.
Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
24 Manus fortium dominabitur: quae autem remissa est, tributis serviet.
Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
25 Moeror in corde viri humiliabit illum, et sermone bono laetificabitur.
Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
26 Qui negligit damnum propter amicum, iustus est: iter autem impiorum decipiet eos.
Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
27 Non inveniet fraudulentus lucrum: et substantia hominis erit auri pretium.
Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
28 In semita iustitiae, vita: iter autem devium ducit ad mortem.
Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.