< Job 9 >

1 Et respondens Iob, ait:
Ndipo Yobu anayankha kuti,
2 Vere scio quod ita sit, et quod non iustificetur homo compositus Deo.
“Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
3 Si voluerit contendere cum eo, non poterit ei respondere unum pro mille.
Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
4 Sapiens corde est, et fortis robore: quis restitit ei, et pacem habuit?
Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
5 Qui transtulit montes, et nescierunt hi quos subvertit in furore suo.
Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
6 Qui commovet terram de loco suo, et columnae eius concutiuntur.
Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
7 Qui praecipit Soli, et non oritur: et stellas claudit quasi sub signaculo:
Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
8 Qui extendit caelos solus, et graditur super fluctus maris.
Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
9 Qui facit Arcturum, et Oriona, et Hyadas, et interiora austri.
Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
10 Qui facit magna, et incomprehensibilia, et mirabilia, quorum non est numerus.
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
11 Si venerit ad me, non videbo eum: si abierit, non intelligam.
Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
12 Si repente interroget, quis respondebit ei? vel quis dicere potest: Cur ita facis?
Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
13 Deus, cuius irae nemo resistere potest, et sub quo curvantur qui portant orbem.
Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
14 Quantus ergo sum ego, ut respondeam ei, et loquar verbis meis cum eo?
“Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
15 Qui etiam si habuero quippiam iustum, non respondebo, sed meum iudicem deprecabor.
Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
16 Et cum invocantem exaudierit me, non credo quod audierit vocem meam.
Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
17 In turbine enim conteret me, et multiplicabit vulnera mea etiam sine causa.
Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
18 Non concedit requiescere spiritum meum, et implet me amaritudinibus.
Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
19 Si fortitudo quaeritur, robustissimus est: si aequitas iudicii, nemo audet pro me testimonium dicere.
Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
20 Si iustificare me voluero, os meum condemnabit me: si innocentem ostendero, pravum me comprobabit.
Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
21 Etiam si simplex fuero, hoc ipsum ignorabit anima mea, et taedebit me vitae meae.
“Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
22 Unum est quod locutus sum, et innocentem et impium ipse consumit.
Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
23 Si flagellat, occidat semel, et non de poenis innocentum rideat.
Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
24 Terra data est in manus impii, vultum iudicum eius operit: quod si non ille est, quis ergo est?
Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
25 Dies mei velociores fuerunt cursore: fugerunt, et non viderunt bonum.
“Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
26 Pertransierunt quasi naves poma portantes, sicut aquila volans ad escam.
Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
27 Cum dixero: Nequaquam ita loquar: commuto faciem meam, et dolore torqueor.
Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
28 Verebar omnia opera mea, sciens quod non parceres delinquenti.
ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
29 Si autem et sic impius sum, quare frustra laboravi?
Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
30 Si lotus fuero quasi aquis nivis, et fulserint velut mundissimae manus meae:
Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
31 Tamen sordibus intinges me, et abominabuntur me vestimenta mea.
mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
32 Neque enim viro qui similis mei est, respondebo: nec qui mecum in iudicio ex aequo possit audiri.
“Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
33 Non est qui utrumque valeat arguere, et ponere manum suam in ambobus.
Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
34 Auferat a me virgam suam, et pavor eius non me terreat.
munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
35 Loquar, et non timebo eum: neque enim possum metuens respondere.
Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.

< Job 9 >