< Job 41 >

1 An extrahere poteris leviathan hamo, et fune ligabis linguam eius?
“Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
2 Numquid pones circulum in naribus eius, aut armilla perforabis maxillam eius?
Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
3 Numquid multiplicabit ad te preces, aut loquetur tibi mollia?
Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
4 Numquid feriet tecum pactum, et accipies eum servum sempiternum?
Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
5 Numquid illudes ei quasi avi, aut ligabis eum ancillis tuis?
Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
6 Concident eum amici, divident illum negotiatores?
Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
7 Numquid implebis sagenas pelle eius, et gurgustium piscium capite illius?
Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
8 Pone super eum manum tuam: memento belli, nec ultra addas loqui.
Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
9 Ecce, spes eius frustrabitur eum, et videntibus cunctis praecipitabitur.
Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
10 Non quasi crudelis suscitabo eum: quis enim resistere potest vultui meo?
Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
11 Quis ante dedit mihi, ut reddam ei? omnia quae sub caelo sunt, mea sunt.
Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
12 Non parcam ei, et verbis potentibus, et ad deprecandum compositis.
“Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
13 Quis revelabit faciem indumenti eius? et in medium oris eius quis intrabit?
Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
14 Portas vultus eius quis aperiet? per gyrum dentium eius formido.
Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
15 Corpus illius quasi scuta fusilia, compactum squamis se prementibus.
Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
16 Una uni coniungitur, et ne spiraculum quidem incedit per eas:
Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
17 Una alteri adhaerebit, et tenentes se nequaquam separabuntur.
Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
18 Sternutatio eius splendor ignis, et oculi eius, ut palpebrae diluculi.
Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
19 De ore eius lampades procedunt, sicut taedae ignis accensae.
Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
20 De naribus eius procedit fumus, sicut ollae succensae atque ferventis.
Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
21 Halitus eius prunas ardere facit, et flamma de ore eius egreditur.
Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
22 In collo eius morabitur fortitudo, et faciem eius praecedit egestas.
Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
23 Membra carnium eius cohaerentia sibi: mittet contra eum flumina, et ad locum alium non ferentur.
Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
24 Cor eius indurabitur tamquam lapis, et stringetur quasi malleatoris incus.
Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
25 Cum sublatus fuerit, timebunt angeli, et territi purgabuntur.
Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
26 Cum apprehenderit eum gladius, subsistere non poterit neque hasta, neque thorax:
Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
27 Reputabit enim quasi paleas ferrum, et quasi lignum putridum, aes.
Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
28 Non fugabit eum vir sagittarius, in stipulam versi sunt ei lapides fundae.
Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
29 Quasi stipulam aestimabit malleum, et deridebit vibrantem hastam.
Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
30 Sub ipso erunt radii solis, et sternet sibi aurum quasi lutum.
Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
31 Fervescere faciet quasi ollam profundum mare, et ponet quasi cum unguenta bulliunt.
Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
32 Post eum lucebit semita, aestimabit abyssum quasi senescentem.
Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
33 Non est super terram potestas, quae comparetur ei, qui factus est ut nullum timeret.
Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
34 Omne sublime videt, ipse est rex super universos filios superbiae.
Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”

< Job 41 >