< Job 36 >
1 Addens quoque Eliu, haec locutus est:
Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
2 Sustine me paululum, et indicabo tibi: adhuc enim habeo quod pro Deo loquar.
“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
3 Repetam scientiam meam a principio, et operatorem meum probabo iustum.
Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
4 Vere enim absque mendacio sermones mei, et perfecta scientia probabitur tibi.
Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
5 Deus potentes non abiicit, cum et ipse sit potens.
“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
6 Sed non salvat impios, et iudicium pauperibus tribuit.
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
7 Non auferet a iusto oculos suos, et reges in solio collocat in perpetuum, et illic eriguntur.
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
8 Et si fuerint in catenis, et vinciantur funibus paupertatis.
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
9 Indicabit eis opera eorum, et scelera eorum, quia violenti fuerunt.
Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 Revelabit quoque aurem eorum, ut corripiat: et loquetur, ut revertantur ab iniquitate.
Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 Si audierint et observaverint, complebunt dies suos in bono, et annos suos in gloria:
Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 Si autem non audierint, transibunt per gladium, et consumentur in stultitia.
Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
13 Simulatores et callidi provocant iram Dei, neque clamabunt cum vincti fuerint.
“Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 Morietur in tempestate anima eorum, et vita eorum inter effeminatos.
Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 Eripiet de angustia sua pauperem, et revelabit in tribulatione aurem eius.
Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
16 Igitur salvabit te de ore angusto latissime, et non habente fundamentum subter se: requies autem mensae tuae erit plena pinguedine.
“Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 Causa tua quasi impii iudicata est, causam iudiciumque recipies.
Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 Non te ergo superet ira, ut aliquem opprimas: nec multitudo donorum inclinet te.
Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 Depone magnitudinem tuam absque tribulatione, et omnes robustos fortitudine.
Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 Ne protrahas noctem, ut ascendant populi pro eis.
Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 Cave ne declines ad iniquitatem: hanc enim coepisti sequi post miseriam.
Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
22 Ecce, Deus excelsus in fortitudine sua, et nullus ei similis in legislatoribus.
“Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 Quis poterit scrutari vias eius? aut quis potest ei dicere: Operatus es iniquitatem?
Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
24 Memento quod ignores opus eius, de quo cecinerunt viri.
Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
25 Omnes homines vident eum, unusquisque intuetur procul.
Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
26 Ecce, Deus magnus vincens scientiam nostram: numerus annorum eius inaestimabilis.
Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
27 Qui aufert stillas pluviae, et effundit imbres ad instar gurgitum.
“Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
28 Qui de nubibus fluunt, quae praetexunt cuncta desuper.
mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
29 Si voluerit extendere nubes quasi tentorium suum.
Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
30 Et fulgurare lumine suo desuper, cardines quoque maris operiet.
Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
31 Per haec enim iudicat populos, et dat escas multis mortalibus.
Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
32 In manibus abscondit lucem, et praecepit ei ut rursus adveniat.
Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
33 Annunciat de ea amico suo, quod possessio eius sit, ut ad eam possit ascendere.
Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.