< Job 33 >

1 Audi igitur Iob eloquia mea, et omnes sermones meos ausculta.
“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
2 Ecce aperui os meum, loquatur lingua mea in faucibus meis.
Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
3 Simplici corde meo sermones mei, et sententiam puram labia mea loquentur.
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
4 Spiritus Dei fecit me, et spiraculum Omnipotentis vivificavit me.
Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
5 Si potes, responde mihi, et adversus faciem meam consiste.
Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
6 Ecce, et me sicut et te fecit Deus, et de eodem luto ego quoque formatus sum.
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
7 Verumtamen miraculum meum non te terreat, et eloquentia mea non sit tibi gravis.
Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
8 Dixisti ergo in auribus meis, et vocem verborum tuorum audivi:
“Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
9 Mundus sum ego, et absque delicto: immaculatus, et non est iniquitas in me.
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
10 Quia querelas in me reperit, ideo arbitratus est me inimicum sibi.
Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
11 Posuit in nervo pedes meos, custodivit omnes semitas meas.
Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
12 Hoc est ergo, in quo non es iustificatus: respondebo tibi, quia maior sit Deus homine.
“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
13 Adversus eum contendis quod non ad omnia verba responderit tibi?
Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
14 Semel loquitur Deus, et secundo idipsum non repetit.
Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
15 Per somnium in visione nocturna, quando irruit sopor super homines, et dormiunt in lectulo:
Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
16 Tunc aperit aures virorum, et erudiens eos instruit disciplina,
amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
17 Ut avertat hominem ab his, quae facit, et liberet eum de superbia:
kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
18 Eruens animam eius a corruptione: et vitam illius, ut non transeat in gladium.
kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
19 Increpat quoque per dolorem in lectulo, et omnia ossa eius marcescere facit.
“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
20 Abominabilis ei fit in vita sua panis, et animae illius cibus ante desiderabilis.
kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
21 Tabescet caro eius, et ossa, quae tecta fuerant, nudabuntur.
Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
22 Appropinquavit corruptioni anima eius, et vita illius mortiferis.
Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
23 Si fuerit pro eo Angelus loquens, unus de millibus, ut annunciet hominis aequitatem:
“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
24 Miserebitur eius, et dicet: Libera eum, ut non descendat in corruptionem: inveni in quo ei propitier.
kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
25 Consumpta est caro eius a suppliciis, revertatur ad dies adolescentiae suae.
pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
26 Deprecabitur Deum, et placabilis ei erit: et videbit faciem eius in iubilo, et reddet homini iustitiam suam.
Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
27 Respiciet homines, et dicet: Peccavi, et vere deliqui, et, ut eram dignus, non recepi.
Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
28 Liberavit animam suam ne pergeret in interitum, sed vivens lucem videret.
Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
29 Ecce, haec omnia operatur Deus tribus vicibus per singulos.
“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
30 Ut revocet animas eorum a corruptione, et illuminet luce viventium.
kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
31 Attende Iob, et audi me: et tace, dum ego loquor.
“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
32 Si autem habes quod loquaris, responde mihi, loquere: volo enim, te apparere iustum.
Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
33 Quod si non habes, audi me: tace, et docebo te sapientiam.
Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”

< Job 33 >