< Job 27 >

1 Addidit quoque Iob, assumens parabolam suam, et dixit:
Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2 Vivit Deus, qui abstulit iudicium meum, et Omnipotens, qui ad amaritudinem adduxit animam meam.
“Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama, Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,
3 Quia donec superest halitus in me, et spiritus Dei in naribus meis,
nthawi zonse pamene ndili ndi moyo, mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,
4 Non loquentur labia mea iniquitatem, nec lingua mea meditabitur mendacium.
pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa, lilime langa silidzayankhula zachinyengo.
5 Absit a me ut iustos vos esse iudicem: donec deficiam, non recedam ab innocentia mea.
Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona; mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.
6 Iustificationem meam, quam coepi tenere, non deseram: neque enim reprehendit me cor meum in omni vita mea.
Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere; chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.
7 Sit ut impius, inimicus meus: et adversarius meus, quasi iniquus.
“Mdani wanga akhale ngati woyipa, wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!
8 Quae est enim spes hypocritae si avare rapiat, et non liberet Deus animam eius?
Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa, pamene Mulungu achotsa moyo wake?
9 Numquid Deus audiet clamorem eius cum venerit super eum angustia?
Kodi Mulungu amamva kulira kwake pamene zovuta zamugwera?
10 Aut poterit in Omnipotente delectari, et invocare Deum omni tempore?
Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse? Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?
11 Docebo vos per manum Dei quae Omnipotens habeat, nec abscondam.
“Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.
12 Ecce, vos omnes nostis, et quid sine causa vana loquimini?
Inu mwadzionera nokha zonsezi. Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?
13 Haec est pars hominis impii apud Deum, et hereditas violentorum, quam ob Omnipotente suscipient.
“Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa, cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.
14 Si multiplicati fuerint filii eius, in gladio erunt, et nepotes eius non saturabuntur pane.
Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo zidzukulu zake zidzasowa zakudya.
15 Qui reliqui fuerint ex eo, sepelientur in interitu, et viduae illius non plorabunt.
Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri, ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.
16 Si comportaverit quasi terram argentum, et sicut lutum praeparaverit vestimenta:
Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi, ndi kukundika zovala ngati mchenga,
17 Praeparabit quidem, sed iustus vestietur illis: et argentum innocens dividet.
zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale, ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.
18 Aedificavit sicut tinea domum suam, et sicut custos fecit umbraculum.
Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche, ili ngati msasa umene mlonda amamanga.
19 Dives cum dormierit, nihil secum auferet: aperiet oculos suos, et nihil inveniet.
Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko; akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.
20 Apprehendet eum quasi aqua inopia, nocte opprimet eum tempestas.
Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula; mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.
21 Tollet eum ventus urens, et auferet, et velut turbo rapiet eum de loco suo.
Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo imamuchotsa pamalo pake.
22 Et mittet super eum, et non parcet: de manu eius fugiens fugiet.
Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni, pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.
23 Stringet super eum manus suas, et sibilabit super illum, intuens locum eius.
Mphepoyo imamuwomba ndithu ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”

< Job 27 >