< Job 20 >

1 Respondens autem Sophar Naamathites, dixit:
Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
2 Idcirco cogitationes meae variae succedunt sibi, et mens in diversa rapitur.
“Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
3 Doctrinam, qua me arguis, audiam, et spiritus intelligentiae meae respondebit mihi.
Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
4 Hoc scio a principio, ex quo positus est homo super terram,
“Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
5 Quod laus impiorum brevis sit, et gaudium hypocritae ad instar puncti.
kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
6 Si ascenderit usque ad caelum superbia eius, et caput eius nubes tetigerit:
Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
7 Quasi sterquilinium in fine perdetur: et qui eum viderant, dicent: Ubi est?
iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
8 Velut somnium avolans non invenietur, transiet sicut visio nocturna.
Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
9 Oculus, qui eum viderat, non videbit, neque ultra intuebitur eum locus suus.
Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
10 Filii eius atterentur egestate, et manus illius reddent ei dolorem suum.
Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
11 Ossa eius implebuntur vitiis adolescentiae eius, et cum eo in pulvere dormient.
Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
12 Cum enim dulce fuerit in ore eius malum, abscondet illud sub lingua sua.
“Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
13 Parcet illi, et non derelinquet illud, et celabit in gutture suo.
ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
14 Panis eius in utero illius vertetur in fel aspidum intrinsecus.
koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
15 Divitias, quas devoravit, evomet, et de ventre illius extrahet eas Deus.
Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
16 Caput aspidum suget, et occidet eum lingua viperae.
Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
17 (Non videat rivulos fluminis, torrentes mellis, et butyri.)
Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
18 Luet quae fecit omnia, nec tamen consumetur: iuxta multitudinem adinventionum suarum, sic et sustinebit.
Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
19 Quoniam confringens nudavit pauperes: domum rapuit, et non aedificavit eam.
Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
20 Nec est satiatus venter eius: et cum habuerit quae concupierat, possidere non poterit.
“Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
21 Non remansit de cibo eius, et propterea nihil permanebit de bonis eius.
Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
22 Cum satiatus fuerit, arctabitur, aestuabit, et omnis dolor irruet super eum.
Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
23 Utinam impleatur venter eius, ut emittat in eum iram furoris sui, et pluat super illum bellum suum.
Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
24 Fugiet arma ferrea, et irruet in arcum aereum.
Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
25 Gladius eductus, et egrediens de vagina sua, et fulgurans in amaritudine sua: vadent, et venient super eum horribiles.
Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
26 Omnes tenebrae absconditae sunt in occultis eius: devorabit eum ignis, qui non succenditur, affligetur relictus in tabernaculo suo.
mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
27 Revelabunt caeli iniquitatem eius, et terra consurget adversus eum.
Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
28 Apertum erit germen domus illius, detrahetur in die furoris Dei.
Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
29 Haec est pars hominis impii a Deo, et hereditas verborum eius a Domino.
Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”

< Job 20 >