< Job 16 >

1 Respondens autem Iob, dixit:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Audivi frequenter talia, consolatores onerosi omnes vos estis.
“Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
3 Numquid habebunt finem verba ventosa? aut aliquid tibi molestum est si loquaris?
Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
4 Poteram et ego similia vestri loqui: atque utinam esset anima vestra pro anima mea: Consolarer et ego vos sermonibus, et moverem caput meum super vos:
Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
5 Roborarem vos ore meo: et moverem labia mea, quasi parcens vobis.
Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
6 Sed quid agam? Si locutus fuero, non quiescet dolor meus: et si tacuero, non recedet a me.
“Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
7 Nunc autem oppressit me dolor meus, et in nihilum redacti sunt omnes artus mei.
Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
8 Rugae meae testimonium dicunt contra me, et suscitatur falsiloquus adversus faciem meam contradicens mihi.
Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
9 Collegit furorem suum in me, et comminans mihi, infremuit contra me dentibus suis: hostis meus terribilibus oculis me intuitus est.
Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
10 Aperuerunt super me ora sua, et exprobrantes percusserunt maxillam meam, satiati sunt poenis meis.
Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
11 Conclusit me Deus apud iniquum, et manibus impiorum me tradidit.
Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
12 Ego ille quondam opulentus repente contritus sum: tenuit cervicem meam, confregit me, et posuit me sibi quasi in signum.
Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
13 Circumdedit me lanceis suis, convulneravit lumbos meos, non pepercit, et effudit in terra viscera mea.
anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
14 Concidit me vulnere super vulnus, irruit in me quasi gigas.
Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
15 Saccum consui super cutem meam, et operui cinere carnem meam.
“Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
16 Facies mea intumuit a fletu, et palpebrae meae caligaverunt.
Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
17 Haec passus sum absque iniquitate manus meae, cum haberem mundas ad Deum preces.
komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
18 Terra ne operias sanguinem meum, neque inveniat in te locum latendi clamor meus.
“Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
19 Ecce enim in caelo testis meus, et conscius meus in excelsis.
Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
20 Verbosi amici mei: ad Deum stillat oculus meus.
Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
21 Atque utinam sic iudicaretur vir cum Deo, quomodo iudicatur filius hominis cum collega suo.
iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
22 Ecce enim breves anni transeunt, et semitam, per quam non revertar, ambulo.
“Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”

< Job 16 >