< Psalmorum 97 >
1 Huic David, quando terra ejus restituta est. Dominus regnavit: exsultet terra; lætentur insulæ multæ.
Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale; magombe akutali akondwere.
2 Nubes et caligo in circuitu ejus; justitia et judicium correctio sedis ejus.
Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira; chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.
3 Ignis ante ipsum præcedet, et inflammabit in circuitu inimicos ejus.
Moto umapita patsogolo pake ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.
4 Illuxerunt fulgura ejus orbi terræ; vidit, et commota est terra.
Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse; dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.
5 Montes sicut cera fluxerunt a facie Domini; a facie Domini omnis terra.
Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova, pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.
6 Annuntiaverunt cæli justitiam ejus, et viderunt omnes populi gloriam ejus.
Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake, ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.
7 Confundantur omnes qui adorant sculptilia, et qui gloriantur in simulacris suis. Adorate eum omnes angeli ejus.
Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi, iwo amene amanyadira mafano; mulambireni, inu milungu yonse!
8 Audivit, et lætata est Sion, et exsultaverunt filiæ Judæ propter judicia tua, Domine.
Ziyoni akumva ndipo akukondwera, midzi ya Yuda ikusangalala chifukwa cha maweruzo anu Yehova.
9 Quoniam tu Dominus altissimus super omnem terram; nimis exaltatus es super omnes deos.
Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi; ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.
10 Qui diligitis Dominum, odite malum: custodit Dominus animas sanctorum suorum; de manu peccatoris liberabit eos.
Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
11 Lux orta est justo, et rectis corde lætitia.
Kuwala kumafika pa anthu olungama, ndi chimwemwe kwa olungama mtima.
12 Lætamini, justi, in Domino, et confitemini memoriæ sanctificationis ejus.
Kondwerani mwa Yehova Inu olungama ndipo tamandani dzina lake loyera.