< Psalmorum 38 >

1 Psalmus David, in rememorationem de sabbato. Domine, ne in furore tuo arguas me, neque in ira tua corripias me:
Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
2 quoniam sagittæ tuæ infixæ sunt mihi, et confirmasti super me manum tuam.
Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
3 Non est sanitas in carne mea, a facie iræ tuæ; non est pax ossibus meis, a facie peccatorum meorum:
Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
4 quoniam iniquitates meæ supergressæ sunt caput meum, et sicut onus grave gravatæ sunt super me.
Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
5 Putruerunt et corruptæ sunt cicatrices meæ, a facie insipientiæ meæ.
Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
6 Miser factus sum et curvatus sum usque in finem; tota die contristatus ingrediebar.
Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
7 Quoniam lumbi mei impleti sunt illusionibus, et non est sanitas in carne mea.
Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
8 Afflictus sum, et humiliatus sum nimis; rugiebam a gemitu cordis mei.
Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
9 Domine, ante te omne desiderium meum, et gemitus meus a te non est absconditus.
Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
10 Cor meum conturbatum est; dereliquit me virtus mea, et lumen oculorum meorum, et ipsum non est mecum.
Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
11 Amici mei et proximi mei adversum me appropinquaverunt, et steterunt; et qui juxta me erant, de longe steterunt: et vim faciebant qui quærebant animam meam.
Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
12 Et qui inquirebant mala mihi, locuti sunt vanitates, et dolos tota die meditabantur.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
13 Ego autem, tamquam surdus, non audiebam; et sicut mutus non aperiens os suum.
Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
14 Et factus sum sicut homo non audiens, et non habens in ore suo redargutiones.
Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
15 Quoniam in te, Domine, speravi; tu exaudies me, Domine Deus meus.
Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
16 Quia dixi: Nequando supergaudeant mihi inimici mei; et dum commoventur pedes mei, super me magna locuti sunt.
Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
17 Quoniam ego in flagella paratus sum, et dolor meus in conspectu meo semper.
Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
18 Quoniam iniquitatem meam annuntiabo, et cogitabo pro peccato meo.
Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
19 Inimici autem mei vivunt, et confirmati sunt super me: et multiplicati sunt qui oderunt me inique.
Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
20 Qui retribuunt mala pro bonis detrahebant mihi, quoniam sequebar bonitatem.
Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
21 Ne derelinquas me, Domine Deus meus; ne discesseris a me.
Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
22 Intende in adjutorium meum, Domine Deus salutis meæ.
Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.

< Psalmorum 38 >