< Psalmorum 114 >
1 Alleluja. In exitu Israël de Ægypto, domus Jacob de populo barbaro,
Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
2 facta est Judæa sanctificatio ejus; Israël potestas ejus.
Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
3 Mare vidit, et fugit; Jordanis conversus est retrorsum.
Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
4 Montes exsultaverunt ut arietes, et colles sicut agni ovium.
mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
5 Quid est tibi, mare, quod fugisti? et tu, Jordanis, quia conversus es retrorsum?
Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
6 montes, exsultastis sicut arietes? et colles, sicut agni ovium?
inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
7 A facie Domini mota est terra, a facie Dei Jacob:
Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
8 qui convertit petram in stagna aquarum, et rupem in fontes aquarum.
amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.