< Proverbiorum 15 >
1 Responsio mollis frangit iram; sermo durus suscitat furorem.
Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo, koma mawu ozaza amautsa ukali.
2 Lingua sapientium ornat scientiam; os fatuorum ebullit stultitiam.
Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.
3 In omni loco, oculi Domini contemplantur bonos et malos.
Maso a Yehova ali ponseponse, amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.
4 Lingua placabilis lignum vitæ; quæ autem immoderata est conteret spiritum.
Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo, koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.
5 Stultus irridet disciplinam patris sui; qui autem custodit increpationes astutior fiet. In abundanti justitia virtus maxima est: cogitationes autem impiorum eradicabuntur.
Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake, koma wochenjera amasamala chidzudzulo.
6 Domus justi plurima fortitudo, et in fructibus impii conturbatio.
Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri, zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.
7 Labia sapientium disseminabunt scientiam; cor stultorum dissimile erit.
Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru; koma mitima ya zitsiru sitero.
8 Victimæ impiorum abominabiles Domino; vota justorum placabilia.
Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.
9 Abominatio est Domino via impii; qui sequitur justitiam diligitur ab eo.
Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.
10 Doctrina mala deserenti viam vitæ; qui increpationes odit, morietur.
Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa. Odana ndi chidzudzulo adzafa.
11 Infernus et perditio coram Domino; quanto magis corda filiorum hominum! (Sheol )
Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova, nanji mitima ya anthu! (Sheol )
12 Non amat pestilens eum qui se corripit, nec ad sapientes graditur.
Wonyoza sakonda kudzudzulidwa; iye sapita kwa anthu anzeru.
13 Cor gaudens exhilarat faciem; in mœrore animi dejicitur spiritus.
Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe, koma mtima wosweka umawawitsa moyo.
14 Cor sapientis quærit doctrinam, et os stultorum pascitur imperitia.
Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.
15 Omnes dies pauperis, mali; secura mens quasi juge convivium.
Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa, koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.
16 Melius est parum cum timore Domini, quam thesauri magni et insatiabiles.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova, kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.
17 Melius est vocari ad olera cum caritate, quam ad vitulum saginatum cum odio.
Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi, kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.
18 Vir iracundus provocat rixas; qui patiens est mitigat suscitatas.
Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano, koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.
19 Iter pigrorum quasi sepes spinarum; via justorum absque offendiculo.
Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga, koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.
20 Filius sapiens lætificat patrem, et stultus homo despicit matrem suam.
Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.
21 Stultitia gaudium stulto, et vir prudens dirigit gressus suos.
Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru, koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.
22 Dissipantur cogitationes ubi non est consilium; ubi vero sunt plures consiliarii, confirmantur.
Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka, koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.
23 Lætatur homo in sententia oris sui, et sermo opportunus est optimus.
Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera, ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.
24 Semita vitæ super eruditum, ut declinet de inferno novissimo. (Sheol )
Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo kuti apewe malo okhala anthu akufa. (Sheol )
25 Domum superborum demolietur Dominus, et firmos faciet terminos viduæ.
Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.
26 Abominatio Domini cogitationes malæ, et purus sermo pulcherrimus firmabitur ab eo.
Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova, koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.
27 Conturbat domum suam qui sectatur avaritiam; qui autem odit munera, vivet. Per misericordiam et fidem purgantur peccata: per timorem autem Domini declinat omnis a malo.
Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake, koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.
28 Mens justi meditatur obedientiam; os impiorum redundat malis.
Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire, koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.
29 Longe est Dominus ab impiis, et orationes justorum exaudiet.
Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa, koma amamva pemphero la anthu olungama.
30 Lux oculorum lætificat animam; fama bona impinguat ossa.
Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.
31 Auris quæ audit increpationes vitæ in medio sapientium commorabitur.
Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo adzakhala pakati pa anthu anzeru.
32 Qui abjicit disciplinam despicit animam suam; qui autem acquiescit increpationibus possessor est cordis.
Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha, koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.
33 Timor Domini disciplina sapientiæ, et gloriam præcedit humilitas.
Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru, ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.