< I Paralipomenon 24 >
1 Porro filiis Aaron hæ partitiones erant. Filii Aaron: Nadab, et Abiu, et Eleazar, et Ithamar.
Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
2 Mortui sunt autem Nadab et Abiu ante patrem suum absque liberis: sacerdotioque functus est Eleazar, et Ithamar.
Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
3 Et divisit eos David, id est, Sadoc de filiis Eleazari, et Ahimelech de filiis Ithamar, secundum vices suas et ministerium.
Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
4 Inventique sunt multo plures filii Eleazar in principibus viris, quam filii Ithamar. Divisit autem eis, hoc est, filiis Eleazar, principes per familias sedecim: et filiis Ithamar per familias et domos suas octo.
Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
5 Porro divisit utrasque inter se familias sortibus: erant enim principes sanctuarii, et principes Dei, tam de filiis Eleazar quam de filiis Ithamar.
Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
6 Descripsitque eos Semeias filius Nathanaël scriba Levites, coram rege et principibus, et Sadoc sacerdote, et Ahimelech filio Abiathar, principibus quoque familiarum sacerdotalium, et Leviticarum: unam domum, quæ ceteris præerat, Eleazar: et alteram domum, quæ sub se habebat ceteros, Ithamar.
Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
7 Exivit autem sors prima Jojarib, secunda Jedei,
Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
8 tertia Harim, quarta Seorim,
achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
9 quinta Melchia, sexta Maiman,
achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
10 septima Accos, octava Abia,
achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
11 nona Jesua, decima Sechenia,
achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
12 undecima Eliasib, duodecima Jacim,
a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
13 tertiadecima Hoppha, decimaquarta Isbaab,
a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
14 decimaquinta Belga, decimasexta Emmer,
a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
15 decimaseptima Hezir, decimaoctava Aphses,
a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
16 decimanona Pheteia, vigesima Hezechiel,
a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
17 vigesima prima Jachin, vigesima secunda Gamul,
a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
18 vigesima tertia Dalaiau, vigesima quarta Maaziau.
a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
19 Hæ vices eorum secundum ministeria sua, ut ingrediantur domum Domini, et juxta ritum suum sub manu Aaron patris eorum, sicut præceperat Dominus Deus Israël.
Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
20 Porro filiorum Levi qui reliqui fuerant, de filiis Amram erat Subaël, et de filiis Subaël, Jehedeia.
Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
21 De filiis quoque Rohobiæ, princeps Jesias.
Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
22 Isaari vero filius Salemoth, filiusque Salemoth Jahath:
Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
23 filiusque ejus Jeriau primus, Amarias secundus, Jahaziel tertius, Jecmaan quartus.
Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
24 Filius Oziel, Micha: filius Micha, Samir.
Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
25 Frater Micha, Jesia: filiusque Jesiæ, Zacharias.
Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
26 Filii Merari: Moholi, et Musi. Filius Oziau: Benno.
Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
27 Filius quoque Merari: Oziau, et Soam, et Zachur, et Hebri.
Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
28 Porro Moholi filius, Eleazar, qui non habebat liberos.
Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
29 Filius vero Cis, Jerameel.
Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
30 Filii Musi: Moholi, Eder et Jerimoth: isti filii Levi secundum domos familiarum suarum.
Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
31 Miseruntque et ipsi sortes contra fratres suos filios Aaron coram David rege, et Sadoc, et Ahimelech, et principibus familiarum sacerdotalium et Leviticarum, tam majores quam minores: omnes sors æqualiter dividebat.
Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.