< Psalmorum 44 >
1 In finem, Filiis Core ad intellectum.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
2 Deus auribus nostris audivimus: patres nostri annunciaverunt nobis. Opus, quod operatus es in diebus eorum: et in diebus antiquis.
Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
3 Manus tua gentes disperdidit, et plantasti eos: afflixisti populos, et expulisti eos:
Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
4 Nec enim in gladio suo possederunt terram, et brachium eorum non salvavit eos: Sed dextera tua, et brachium tuum, et illuminatio vultus tui: quoniam complacuisti in eis.
Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
5 Tu es ipse rex meus et Deus meus: qui mandas salutes Iacob.
Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
6 In te inimicos nostros ventilabimus cornu, et in nomine tuo spernemus insurgentes in nobis.
Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
7 Non enim in arcu meo sperabo: et gladius meus non salvabit me.
koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
8 Salvasti enim nos de affligentibus nos: et odientes nos confudisti.
Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
9 In Deo laudabimur tota die: et in nomine tuo confitebimur in sæculum.
Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
10 Nunc autem repulisti et confudisti nos: et non egredieris Deus in virtutibus nostris.
Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
11 Avertisti nos retrorsum post inimicos nostros: et qui oderunt nos, diripiebant sibi.
Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
12 Dedisti nos tamquam oves escarum: et in gentibus dispersisti nos.
Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
13 Vendidisti populum tuum sine pretio: et non fuit multitudo in commutationibus eorum.
Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
14 Posuisti nos opprobrium vicinis nostris, subsannationem et derisum his, qui sunt in circuitu nostro.
Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
15 Posuisti nos in similitudinem Gentibus: commotionem capitis in populis.
Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
16 Tota die verecundia mea contra me est, et confusio faciei meæ cooperuit me.
chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
17 A voce exprobrantis, et obloquentis: a facie inimici, et persequentis.
Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
18 Hæc omnia venerunt super nos, nec obliti sumus te: et inique non egimus in testamento tuo.
Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
19 Et non recessit retro cor nostrum: et declinasti semitas nostras a via tua:
Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
20 Quoniam humiliasti nos in loco afflictionis, et cooperuit nos umbra mortis.
Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
21 Si obliti sumus nomen Dei nostri, et si expandimus manus nostras ad deum alienum:
kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
22 Nonne Deus requiret ista? ipse enim novit abscondita cordis. Quoniam propter te mortificamur tota die: æstimati sumus sicut oves occisionis.
Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
23 Exurge, quare obdormis Domine? exurge, et ne repellas in finem.
Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
24 Quare faciem tuam avertis, oblivisceris inopiæ nostræ et tribulationis nostræ?
Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
25 Quoniam humiliata est in pulvere anima nostra: conglutinatus est in terra venter noster.
Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
26 Exurge Domine, adiuva nos: et redime nos propter nomen tuum.
Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.