< Psalmorum 50 >

1 Psalmus Asaph. Deus deorum Dominus locutus est: et vocavit terram, A solis ortu usque ad occasum:
Salimo la Asafu. Wamphamvuyo, Yehova Mulungu, akuyankhula ndi kuyitanitsa dziko lapansi kuyambira kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.
2 ex Sion species decoris eius.
Kuchokera ku Ziyoni, mokongola kwambiri Mulungu akuwala.
3 Deus manifeste veniet: Deus noster et non silebit. Ignis in conspectu eius exardescet: et in circuitu eius tempestas valida.
Mulungu wathu akubwera ndipo sadzakhala chete; moto ukunyeketsa patsogolo pake, ndipo pomuzungulira pali mphepo yamkuntho
4 Advocabit cælum desursum: et terram discernere populum suum.
Iye akuyitanitsa zamumlengalenga ndi za pa dziko lapansi kuti aweruze anthu ake.
5 Congregate illi sanctos eius: qui ordinant testamentum eius super sacrificia.
Mundisonkhanitsire okhulupirika anga, amene anachita pangano ndi ine pochita nsembe.
6 Et annunciabunt cæli iustitiam eius: quoniam Deus iudex est.
Ndipo mayiko akumwamba akulengeza chilungamo chake, pakuti Mulungu mwini ndi woweruza.
7 Audi populus meus, et loquar: Israel, et testificabor tibi: Deus, Deus tuus ego sum.
Imvani inu anthu anga, ndipo Ine ndidzayankhula, iwe Israeli, ndipo Ine ndidzayankhula mokutsutsa; ndine Mulungu, Mulungu wako.
8 Non in sacrificiis tuis arguam te: holocausta autem tua in conspectu meo sunt semper.
Sindikudzudzula chifukwa cha nsembe zako, kapena nsembe zako zopsereza zimene zili pamaso panga nthawi zonse.
9 Non accipiam de domo tua vitulos: neque de gregibus tuis hircos.
Ine sindikufuna ngʼombe yayimuna kuchokera mʼkhola lako kapena mbuzi za mʼkhola lako,
10 Quoniam meæ sunt omnes feræ silvarum, iumenta in montibus et boves.
pakuti nyama iliyonse yakunkhalango ndi yanga ndiponso ngʼombe za ku mapiri ochuluka.
11 Cognovi omnia volatilia cæli: et pulchritudo agri mecum est.
Ine ndimadziwa mbalame iliyonse mʼmapiri ndiponso zolengedwa zonse zakutchire ndi zanga.
12 Si esuriero, non dicam tibi: meus est enim orbis terræ, et plenitudo eius.
Ndikanakhala ndi njala sindikanakuwuzani, pakuti dziko lonse ndi zonse zimene zili mʼmenemo ndi zanga.
13 Numquid manducabo carnes taurorum? aut sanguinem hircorum potabo?
Kodi ndimadya nyama ya ngʼombe zazimuna kapena kumwa magazi a mbuzi?
14 Immola Deo sacrificium laudis: et redde Altissimo vota tua.
“Pereka nsembe zachiyamiko kwa Mulungu, kwaniritsa malonjezo ako kwa Wammwambamwamba.
15 Et invoca me in die tribulationis: eruam te, et honorificabis me.
Ndipo undiyitane pa tsiku lako la masautso; Ine ndidzakulanditsa, ndipo udzandilemekeza.”
16 Peccatori autem dixit Deus: Quare tu enarras iustitias meas, et assumis testamentum meum per os tuum?
Koma kwa woyipa, Mulungu akuti, “Kodi uli ndi mphamvu yanji kuti uzinena malamulo anga kapena kutenga pangano langa pa milomo yako?
17 Tu vero odisti disciplinam: et proiecisti sermones meos retrorsum:
Iwe umadana ndi malangizo anga ndipo umaponyera kumbuyo kwako mawu anga.
18 Si videbas furem, currebas cum eo: et cum adulteris portionem tuam ponebas.
Ukaona wakuba umamutsatira, umachita maere ako pamodzi ndi achigololo
19 Os tuum abundavit malitia: et lingua tua concinnabat dolos.
Umagwiritsa ntchito pakamwa pako pa zinthu zoyipa ndipo umakonza lilime lako kuchita chinyengo.
20 Sedens adversus fratrem tuum loquebaris, et adversus filium matris tuæ ponebas scandalum:
Nthawi zonse umayankhula motsutsana ndi mʼbale wako ndipo umasinjirira mwana wa amayi ako enieni.
21 hæc fecisti, et tacui. Existimasti inique quod ero tui similis: arguam te, et statuam contra faciem tuam.
Wachita zimenezi ndipo Ine ndinali chete; umaganiza kuti ndine wofanana nawe koma ndidzakudzudzula ndipo ndidzakutsutsa pamaso pako.
22 Intelligite hæc qui obliviscimini Deum: nequando rapiat, et non sit qui eripiat.
“Ganizira izi, iwe amene umayiwala Mulungu kuti ndingakukadzule popanda wokupulumutsa:
23 Sacrificium laudis honorificabit me: et illic iter, quo ostendam illi salutare Dei.
Iye amene amapereka nsembe yamayamiko amandilemekeza, ndipo amakonza njira zake kuti ndimuonetse chipulumutso cha Mulungu.”

< Psalmorum 50 >