< Proverbiorum 8 >

1 Numquid non sapientia clamitat, et prudentia dat vocem suam?
Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
2 In summis, excelsisque verticibus supra viam, in mediis semitis stans,
Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
3 iuxta portas civitatis in ipsis foribus loquitur, dicens:
Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
4 O viri, ad vos clamito, et vox mea ad filios hominum.
Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
5 Intelligite parvuli astutiam, et insipientes animadvertite.
Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
6 Audite, quoniam de rebus magnis locutura sum: et aperientur labia mea, ut recta prædicent.
Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
7 Veritatem meditabitur guttur meum, et labia mea detestabuntur impium.
Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
8 Iusti sunt omnes sermones mei, non est in eis pravum quid, neque perversum.
Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
9 Recti sunt intelligentibus, et æqui invenientibus scientiam.
Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
10 Accipite disciplinam meam, et non pecuniam: doctrinam magis, quam aurum eligite.
Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
11 Melior est enim sapientia cunctis pretiosissimis: et omne desiderabile ei non potest comparari.
Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
12 Ego sapientia habito in consilio, et eruditis intersum cogitationibus.
Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
13 Timor Domini odit malum: arrogantiam, et superbiam, et viam pravam, et os bilingue detestor.
Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
14 Meum est consilium, et æquitas, mea est prudentia, mea est fortitudo.
Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
15 Per me reges regnant, et legum conditores iusta decernunt:
Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
16 Per me principes imperant, et potentes decernunt iustitiam.
Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
17 Ego diligentes me diligo: et qui mane vigilant ad me, invenient me.
Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
18 Mecum sunt divitiæ, et gloria, opes superbæ, et iustitia.
Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
19 Melior est enim fructus meus auro, et lapide pretioso, et genimina me argento electo.
Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
20 In viis iustitiæ ambulo, in medio semitarum iudicii,
Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
21 ut ditem diligentes me, et thesauros eorum repleam.
Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
22 Dominus possedit me in initio viarum suarum, antequam quidquam faceret a principio.
“Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
23 Ab æterno ordinata sum, et ex antiquis antequam terra fieret.
Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
24 Nondum erant abyssi, et ego iam concepta eram: necdum fontes aquarum eruperant:
Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
25 necdum montes gravi mole constiterant: ante colles ego parturiebar:
Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
26 adhuc terram non fecerat, et flumina, et cardines orbis terræ.
lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
27 Quando præparabat cælos, aderam: quando certa lege, et gyro vallabat abyssos:
Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
28 quando æthera firmabat sursum, et librabat fontes aquarum:
pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
29 quando circumdabat mari terminum suum, et legem ponebat aquis, ne transirent fines suos: quando appendebat fundamenta terræ:
pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
30 Cum eo eram cuncta componens: et delectabar per singulos dies, ludens coram eo omni tempore;
Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
31 ludens in orbe terrarum: et deliciæ meæ esse, cum filiis hominum.
Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
32 Nunc ergo filii audite me: Beati, qui custodiunt vias meas.
“Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
33 Audite disciplinam, et estote sapientes, et nolite abiicere eam.
Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
34 Beatus homo qui audit me, et qui vigilat ad fores meas quotidie, et observat ad postes ostii mei.
Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
35 Qui me invenerit, inveniet vitam, et hauriet salutem a Domino:
Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
36 qui autem in me peccaverit, lædet animam suam. Omnes, qui me oderunt, diligunt mortem.
Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”

< Proverbiorum 8 >