< Proverbiorum 2 >

1 Fili mi, si susceperis sermones meos, et mandata mea absconderis penes te,
Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
2 ut audiat sapientiam auris tua: inclina cor tuum ad cognoscendam prudentiam.
ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
3 Si enim sapientiam invocaveris, et inclinaveris cor tuum prudentiæ:
ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
4 si quæsieris eam quasi pecuniam, et sicut thesauros effoderis illam:
ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
5 tunc intelliges timorem Domini, et scientiam Dei invenies:
ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
6 quia Dominus dat sapientiam: et ex ore eius prudentia, et scientia.
Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
7 Custodiet rectorum salutem, et proteget gradientes simpliciter,
Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
8 servans semitas iustitiæ, et vias sanctorum custodiens.
pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
9 Tunc intelliges iustitiam, et iudicium, et æquitatem, et omnem semitam bonam.
Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
10 Si intraverit sapientia cor tuum, et scientia animæ tuæ placuerit:
Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
11 consilium custodiet te, et prudentia servabit te,
Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
12 ut eruaris a via mala, et ab homine, qui perversa loquitur:
Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
13 qui relinquunt iter rectum, et ambulant per vias tenebrosas:
amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
14 qui lætantur cum malefecerint, et exultant in rebus pessimis:
amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
15 quorum viæ perversæ sunt, et infames gressus eorum.
Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
16 Ut eruaris a muliere aliena, et ab extranea, quæ mollit sermones suos,
Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
17 et relinquit Ducem pubertatis suæ,
amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
18 et pacti Dei sui oblita est. Inclinata est enim ad mortem domus eius, et ad inferos semitæ ipsius. (questioned)
Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
19 Omnes, qui ingrediuntur ad eam, non revertentur, nec apprehendent semitas vitæ.
Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
20 Ut ambules in via bona: et calles iustorum custodias.
Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
21 Qui enim recti sunt, habitabunt in terra, et simplices permanebunt in ea.
Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
22 Impii vero de terra perdentur: et qui inique agunt, auferentur ex ea.
Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.

< Proverbiorum 2 >