< Lamentationes 3 >

1 ALEPH. Ego vir videns paupertatem meam in virga indignationis eius.
Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
2 ALEPH. Me minavit, et adduxit in tenebras, et non in lucem.
Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
3 ALEPH. Tantum in me vertit, et convertit manum suam tota die.
zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
4 BETH. Vetustam fecit pellem meam, et carnem meam, contrivit ossa mea.
Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
5 BETH. Ædificavit in gyro meo, et circumdedit me felle, et labore.
Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
6 BETH. In tenebrosis collocavit me, quasi mortuos sempiternos.
Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
7 GHIMEL. Circumædificavit adversum me, ut non egrediar: aggravavit compedem meum.
Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
8 GHIMEL. Sed et cum clamavero, et rogavero, exclusit orationem meam.
Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
9 GHIMEL. Conclusit vias meas lapidibus quadris, semitas meas subvertit.
Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
10 DALETH. Ursus insidians factus est mihi: leo in absconditis.
Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
11 DALETH. Semitas meas subvertit, et confregit me: posuit me desolatam.
Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
12 DALETH. Tetendit arcum suum, et posuit me quasi signum ad sagittam.
Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
13 HE. Misit in renibus meis filias pharetræ suæ.
Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
14 HE. Factus sum in derisum omni populo meo, canticum eorum tota die.
Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
15 HE. Replevit me amaritudinibus, inebriavit me absynthio.
Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
16 VAU. Et fregit ad numerum dentes meos, cibavit me cinere.
Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
17 VAU. Et repulsa est a pace anima mea, oblitus sum bonorum.
Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
18 VAU. Et dixi: Periit finis meus, et spes mea a Domino.
Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
19 ZAIN. Recordare paupertatis, et transgressionis meæ, absinthii, et fellis.
Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
20 ZAIN. Memoria memor ero, et tabescet in me anima mea.
Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
21 ZAIN. Hæc recolens in corde meo, ideo sperabo.
Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
22 HETH. Misericordiæ Domini quia non sumus consumpti: quia non defecerunt miserationes eius.
Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
23 HETH. Novi diluculo, multa est fides tua.
Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
24 HETH. Pars mea Dominus, dixit anima mea: propterea expectabo eum.
Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
25 TETH. Bonus est Dominus sperantibus in eum, animæ quærenti illum.
Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
26 TETH. Bonum est præstolari cum silentio salutare Dei.
nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
27 TETH. Bonum est viro, cum portaverit iugum ab adolescentia sua.
Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
28 IOD. Sedebit solitarius, et tacebit: quia levavit super se.
Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
29 IOD. Ponet in pulvere os suum, si forte sit spes.
Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
30 IOD. Dabit percutienti se maxillam, saturabitur opprobriis.
Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
31 CAPH. Quia non repellet in sempiternum Dominus.
Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
32 CAPH. Quia si abiecit, et miserebitur secundum multitudinem misericordiarum suarum.
Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
33 CAPH. Non enim humiliavit ex corde suo, et abiecit filios hominum,
Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
34 LAMED. Ut conteret sub pedibus suis omnes vinctos terræ,
Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
35 LAMED. Ut declinaret iudicium viri in conspectu vultus Altissimi.
kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
36 LAMED. Ut perverteret hominem in iudicio suo, Dominus ignoravit.
kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
37 MEM. Quis est iste, qui dixit ut fieret, Domino non iubente?
Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
38 MEM. Ex ore Altissimi non egredientur nec mala nec bona?
Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
39 MEM. Quid murmuravit homo vivens, vir pro peccatis suis?
Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
40 NUN. Scrutemur vias nostras, et quæramus, et revertamur ad Dominum.
Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
41 NUN. Levemus corda nostra cum manibus ad Dominum in cælos.
Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
42 NUN. Nos inique egimus, et ad iracundiam provocavimus: idcirco tu inexorabilis es.
“Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
43 SAMECH. Operuisti in furore, et percussisti nos: occidisti, nec pepercisti.
“Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
44 SAMECH. Opposuisti nubem tibi, ne transeat oratio.
Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
45 SAMECH. Eradicationem, et abiectionem posuisti me in medio populorum.
Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
46 PHE. Aperuerunt super nos os suum omnes inimici.
“Adani anthu atitsekulira pakamwa.
47 PHE. Formido, et laqueus facta est nobis vaticinatio, et contritio.
Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
48 PHE. Divisiones aquarum deduxit oculus meus, in contritione filiæ populi mei.
Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
49 AIN. Oculus meus afflictus est, nec tacuit, eo quod non esset requies,
Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
50 AIN. Donec respiceret et videret Dominus de cælis.
mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
51 AIN. Oculus meus deprædatus est animam meam in cunctis filiabus urbis meæ.
Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
52 SADE. Venatione ceperunt me quasi avem inimici mei gratis.
Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
53 SADE. Lapsa est in lacum vita mea, et posuerunt lapidem super me.
Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
54 SADE. Inundaverunt aquæ super caput meum: dixi: Perii.
madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
55 COPH. Invocavi nomen tuum Domine de lacu novissimo.
Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
56 COPH. Vocem meam audisti: ne avertas aurem tuam a singultu meo, et clamoribus.
Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
57 COPH. Appropinquasti in die, quando invocavi te: dixisti: Ne timeas.
Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
58 RES. Iudicasti Domine causam animæ meæ, Redemptor vitæ meæ.
Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
59 RES. Vidisti Domine iniquitatem illorum adversum me: iudica iudicium meum.
Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
60 RES. Vidisti omnem furorem, universas cogitationes eorum adversum me.
Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
61 SIN. Audisti opprobrium eorum Domine, omnes cogitationes eorum adversum me:
Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
62 SIN. Labia insurgentium mihi; et meditationes eorum adversum me tota die.
manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
63 SIN. Sessionem eorum, et resurrectionem eorum vide, ego sum psalmus eorum.
Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
64 THAU. Redes eis vicem Domine iuxta opera manuum suarum.
Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
65 THAU. Dabis eis scutum cordis laborem tuum.
Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
66 THAU. Persequeris in furore, et conteres eos sub cælis Domine.
Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.

< Lamentationes 3 >