< Job 40 >
1 Et adiecit Dominus, et locutus est ad Iob:
Yehova anati kwa Yobu:
2 Numquid qui contendit cum Deo, tam facile conquiescit? utique qui arguit Deum, debet respondere ei.
“Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
3 Respondens autem Iob Domino, dixit:
Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
4 Qui leviter locutus sum, respondere quid possum? manum meam ponam super os meum.
“Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
5 Unum locutus sum, quod utinam non dixissem: et alterum, quibus ultra non addam.
Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
6 Respondens autem Dominus Iob de turbine, dixit:
Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
7 Accinge sicut vir lumbos tuos: interrogabo te: et indica mihi.
“Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
8 Numquid irritum facies iudicium meum: et condemnabis me, ut te iustificeris?
“Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
9 Et si habes brachium sicut Deus, et si voce simili tonas?
Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
10 Circumda tibi decorem, et in sublime erigere, et esto gloriosus, et speciosis induere vestibus.
Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
11 Disperge superbos in furore tuo, et respiciens omnem arrogantem humilia.
Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
12 Respice cunctos superbos, et confunde eos, et contere impios in loco suo.
Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
13 Absconde eos in pulvere simul, et facies eorum demerge in foveam:
Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
14 Et ego confitebor quod salvare te possit dextera tua.
Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
15 Ecce, Behemoth, quem feci tecum, fœnum quasi bos comedet:
“Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
16 Fortitudo eius in lumbis eius, et virtus illius in umbilico ventris eius.
Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
17 Stringit caudam suam quasi cedrum, nervi testiculorum eius perplexi sunt.
Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
18 Ossa eius velut fistulæ æris, cartilago illius quasi laminæ ferreæ.
Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
19 Ipse est principium viarum Dei, qui fecit eum, applicabit gladium eius.
Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
20 Huic montes herbas ferunt: omnes bestiæ agri ludent ibi.
Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
21 Sub umbra dormit in secreto calami, et in locis humentibus.
Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
22 Protegunt umbræ umbram eius, circumdabunt eum salices torrentis.
Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
23 Ecce, absorbebit fluvium, et non mirabitur: et habet fiduciam quod influat Iordanis in os eius.
Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
24 In oculis eius quasi hamo capiet eum, et in sudibus perforabit nares eius.
Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?